< Amos 8 >
1 The Lord God schewide to me these thingis; and lo! an hook of applis.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
2 And the Lord seide, What seist thou, Amos? And Y seide, An hook of applis. And the Lord seide to me, The ende is comun on my puple Israel; Y schal no more putte to, that Y passe bi hym.
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 And the herris, ether twistis, of the temple schulen greetli sowne in that dai, seith the Lord God. Many men schulen die, silence schal be cast forth in ech place.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Here ye this thing, whiche al to-breken a pore man, and maken nedi men of the lond for to faile;
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 and ye seien, Whanne schal heruest passe, and we schulen sille marchaundises? and the sabat, and we schulen opene wheete? that we make lesse the mesure, and encreesse the cicle, and `vndur put gileful balauncis;
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 that we welde bi siluer nedi men and pore men for schoon, and we sille outcastyngis of wheete?
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 The Lord swoor ayens the pride of Jacob, Y schal not foryete til to the ende alle the werkis of hem.
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 Whether on this thing the erthe schal not be mouyd togidere, and eche dwellere therof schal mourene? And it schal stie vp as al the flood, and schal be cast out, and schal flete awei as the stronde of Egipt.
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 And it schal be, seith the Lord, in that dai the sunne schal go doun in myddai, and Y schal make the erthe for to be derk in the dai of liyt.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 And Y schal conuerte youre feeste daies in to mourenyng, and alle youre songis in to weilyng; and Y schal brynge yn on ech bac of you a sak, and on ech heed of you ballidnesse; and Y schal put it as the mourenyng of oon bigetun sone, and the laste thingis therof as a bittir dai.
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 Lo! the daies comen, seith the Lord, and Y schal sende out hungur in to erthe; not hungur of breed, nether thirst of watir, but of herynge the word of God.
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 And thei schulen be mouyd to gidere fro the see til to the see, and fro the north til to the eest thei schulen cumpasse, sekynge the word of the Lord, and thei schulen not fynde.
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
13 In that dai faire maidens schulen faile, and yonge men in thirst, whiche sweren in trespas of Samarie,
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
14 and seien, Dan, thi god lyueth, and the weie of Bersabee lyueth; and thei schulen falle, and thei schulen no more rise ayen.
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”