< Amos 5 >
1 Here ye this word, for Y reise on you a weilyng.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 The hous of Israel felle doun, he schal not put to, that it rise ayen; the virgyn of Israel is cast doun in to hir lond, noon is that schal reise hir.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 For the Lord God seith these thingis, The citee of which a thousynde wenten out, an hundrid schulen be left ther ynne; and of which an hundrid wenten out, ten schulen be left ther ynne, in the hous of Israel.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 For the Lord seith these thingis to the hous of Israel, Seke ye me, and ye schulen lyue;
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 and nyle ye seke Bethel, and nyle ye entre in to Galgala, and ye schulen not passe to Bersabee; for whi Galgal schal be led caitif, and Bethel schal be vnprofitable.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Seke ye the Lord, and lyue ye, lest perauenture the hous of Joseph be brent as fier; and it schal deuoure Bethel, and there schal not be, that schal quenche.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 Whiche conuerten doom in to wermod, and forsaken riytwisnesse in the lond,
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 and forsaken hym that makith Arture and Orion, and hym that turneth derknessis in to the morewtid, and him that chaungith dai in to niyt; which clepith watris of the see, and heldith out hem on the face of erthe; the Lord is name of hym.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Which scorneth distriyng on the stronge, and bringith robbyng on the myyti.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Thei hatiden a man repreuynge in the yate, and thei wlatiden a man spekynge perfitli.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Therfor for that that ye robbiden a pore man, and token fro hym the chosun prey, ye schulen bilde housis with square stoon, and ye schulen not dwelle in hem; ye schulen plaunte moost louyd vyneyerdis, and ye schulen not drynke the wyn of hem.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 For Y knew youre grete trespassis many, and youre stronge synnes; enemyes of `the riytwis man, takynge yifte, and berynge doun pore men in the yate.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Therfor a prudent man schal be stille in that time, for the time is yuel.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Seke ye good, and not yuel, that ye lyue, and the Lord God of oostis schal be with you, as ye seiden.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Hate ye yuel, and loue ye good, and ordeyne ye in the gate doom; if perauenture the Lord God of oostis haue merci on the remenauntis of Joseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Therfor the Lord God of oostis, hauynge lordschipe, seith these thingis, Weilyng schal be in alle stretis, and in alle thingis that ben withoutforth it schal be seid, Wo! wo! and thei schulen clepe an erthe tilier to mourenyng, and hem that kunnen weile, to weilyng.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 And weilyng schal be in alle weies, for Y schal passe forth in the myddil of `the see, seith the Lord.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Wo to hem that desiren the dai of the Lord; wher to desiren ye it to you? This dai of the Lord schal be derknessis, and not liyt.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 As if a man renne fro the face of a lioun, and a bere renne to hym; and he entre in to the hous, and lene with his hond on the wal, and a serpent dwellynge in schadewe bite hym.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Whether the dai of the Lord schal not be derknessis, and not liyt; and myist, and not schynyng ther ynne?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Y hatide and castide awei youre feeste daies, and Y schal not take the odour of youre cumpenyes.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 That if ye offren to me youre brent sacrifices, and yiftis, Y schal not resseyue, and Y schal not biholde avowis of youre fatte thingis.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Do thou awei fro me the noise of thi songis, and Y schal not here the songis of thin harpe.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 And doom schal be schewid as watir, and riytfulnesse as a strong streem.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Whether ye, the hous of Israel, offriden to me sacrifices for enemyes to be ouercomun, and sacrifice in desert fourti yeeris?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 And ye han bore tabernaclis to Moloch, youre god, and ymage of youre idols, the sterre of youre god, which ye maden to you.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 And Y schal make you for to passe ouer Damask, seide the Lord; God of oostis is the name of him.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.