< Acts 2 >
1 And whanne the daies of Pentecost weren fillid, alle the disciplis weren togidre in the same place.
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 And sodeynli ther was maad a sown fro heuene, as of a greet wynde comynge, and it fillide al the hous where thei saten.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 And diuerse tungis as fier apperiden to hem, and it sat on ech of hem.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 And alle weren fillid with the Hooli Goost, and thei bigunnen to speke diuerse langagis, as the Hooli Goost yaf to hem for to speke.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 And ther weren in Jerusalem dwellinge Jewis, religiouse men, of ech nacioun that is vndur heuene.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 And whanne this vois was maad, the multitude cam togidere, and thei weren astonyed in thouyt, for ech man herde hem spekinge in his langage.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 And alle weren astonyed, and wondriden, and seiden togidere, Whether not alle these that speken ben men of Galyle,
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 and hou herden we ech man his langage in which we ben borun?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthi, and Medi, and Elamyte, and thei that dwellen at Mesopotami, Judee, and Capodosie, and Ponte,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 and Asie, Frigie, and Pamfilie, Egipt, and the parties of Libie, that is aboue Sirenen, and `comelingis Romayns, and Jewis,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 and proselitis, men of Crete, and of Arabie, we han herd hem spekynge in oure langagis the grete thingis of God.
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 And alle weren astonyed, and wondriden, `and seiden togidere, What wole this thing be?
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 And othere scorneden, and seiden, For these men ben ful of must.
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 But Petre stood with the enleuene, and reiside vp his vois, and spak to hem, Ye Jewis, and alle that dwellen at Jerusalem, be this knowun to you, and with eris perseyue ye my wordis.
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 For not as ye wenen, these ben dronkun, whanne it is the thridde our of the dai;
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 but this it is, that was seid bi the prophete Johel,
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 And it schal be in the laste daies, the Lord seith, Y schal helde out my spirit on ech fleisch; and youre sones and youre douytris schulen prophesie, and youre yonge men schulen se visiouns, and youre eldris schulen dreme sweuenes.
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 And on my seruauntis and myn handmaidens in tho daies Y schal schede out of my spirit, and thei schulen prophecie.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 And Y schal yyue grete wondris in heuene aboue, and signes in erthe bynethe, blood, and fier, and heete of smoke.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 The sunne schal be turned in to derknessis, and the moone in to blood, bifor that the greet and the opyn dai of the Lord come.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 And it schal be, ech man which euere schal clepe to help the name of the Lord, schal be saaf.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 Ye men of Israel, here ye these wordis. Jhesu of Nazareth, a man preued of God bifor you bi vertues, and wondris, and tokenes, which God dide bi hym in the myddil of you,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 as ye witen, ye turmentiden, and killiden hym bi the hoondis of wyckid men, bi counseil determyned and bitakun bi the forknouwyng of God.
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 Whom God reiside, whanne sorewis of helle weren vnboundun, bi that that it was impossible that he were holdun of it.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 For Dauid seith of hym, Y saiy afer the Lord bifore me euermore, for he is on my riythalf, that Y be not mouyd.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 For this thing myn herte ioiede, and my tunge made ful out ioye, and more ouere my fleisch schal reste in hope.
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 For thou schalt not leeue my soule in helle, nethir thou schalt yiue thin hooli to se corrupcioun. (Hadēs )
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs )
28 Thou hast maad knowun to me the weies of lijf, thou schalt fille me in myrthe with thi face.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 Britheren, be it leueful boldli to seie to you of the patriark Dauid, for he is deed and biried, and his sepulcre is among vs in to this dai.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 Therfore whanne he was a prophete, and wiste, that with a greet ooth God hadde sworn to hym, that of the fruyt of his leende schulde oon sitte on his seete,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 he seynge afer spak of the resurreccioun of Crist, for nether he was left in helle, nether his fleisch saiy corrupcioun. (Hadēs )
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs )
32 God reiside this Jhesu, to whom we alle ben witnessis.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Therfor he was enhaunsid bi the riythoond of God, and thorouy the biheest of the Hooli Goost that he took of the fadir, he schedde out this spirit, that ye seen and heren.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 For Dauid stiede not in to heuene; but he seith, The Lord seide to my Lord,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 Sitte thou on my riyt half, til Y putte thin enemyes a stool of thi feet.
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 Therfor moost certeynli wite al the hous of Israel, that God made hym bothe Lord and Crist, this Jhesu, whom ye crucefieden.
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 Whanne thei herden these thingis, thei weren compunct in herte; and thei seiden to Petre and othere apostlis, Britheren, what schulen we do?
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 And Petre seide to hem, Do ye penaunce, and eche of you be baptisid in the name of Jhesu Crist, in to remissioun of youre synnes; and ye schulen take the yifte of the Hooli Goost.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 For the biheest is to you, and to youre sones, and to alle that ben fer, which euer oure Lord God hath clepid.
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 Also with othere wordis ful many he witnesside to hem, and monestide hem, and seide, Be ye sauyd fro this schrewid generacioun.
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 Thanne thei that resseyueden his word weren baptisid, and in that dai soulis weren encreesid, aboute thre thousinde;
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 and weren lastynge stabli in the teching of the apostlis, and in comynyng of the breking of breed, in preieris.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 And drede was maad to ech man. And many wondris and signes weren don bi the apostlis in Jerusalem, and greet drede was in alle.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 And alle that bileueden weren togidre, and hadden alle thingis comyn.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 Thei selden possessiouns and catel, and departiden tho thingis to alle men, as it was nede to ech.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 And ech dai thei dwelliden stabli with o wille in the temple, and braken breed aboute housis, and token mete with ful out ioye and symplenesse of herte,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 and herieden togidere God, and hadden grace to al the folk. And the Lord encreside hem that weren maad saaf, ech dai in to the same thing.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.