< 2 Samuel 23 >

1 Forsothe these ben the laste wordis, whiche Dauid, the sone of Ysai, seide. The man seide, to whom it is ordeyned of Crist, of the God of Jacob, the noble salm makere of Israel;
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 The spiryt of the Lord spak bi me, and his word bi my tunge.
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 Dauid seide, God of Israel spak to me, the stronge of Israel, the `iust Lord of men, `is Lord in the drede of God.
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 As the liyt of the morewtid, whanne the sunne risith eerli, is briyt with out cloudis; and as an erbe cometh forth of the erthe bi reynes.
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 And myn hows is not so greet anentis God, that he schulde make with me euerlastynge couenaunt, stidefast and maad strong in alle thingis; for al myn helthe hangith of him, and al the wille `that is, al my desir, goith in to hym, and no thing is therof, that makith not fruyt.
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 Forsothe alle trespassouris schulen be drawun out as thornes, that ben not takun with hondis.
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 And if ony man wole touche tho, he schal be armed with irun, and with tre formed in to spere; and the thornes schulen be kyndlid, and schulen be brent `til to nouyt.
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 These ben the names of the stronge men of Dauid. Dauid sittith in the chaier, the wiseste prince among thre; he is as a moost tendir worm of tree, that killide eiyte hundrid with o fersnesse.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 Aftir hym was Eleazar, the sone of his fadirs brother Abohi; among thre stronge men, that weren with Dauid, whanne thei seiden schenschip to Filisteis, and weren gaderid thidir in to batel.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 And whanne the men of Israel hadden stied, he stood, and smoot Filisties, til his hond failide, and was starke with the swerd. And the Lord made greet helthe in that dai; and the puple that fledde turnedc ayen to drawe awei the spuylis of slayn men.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 And aftir hym was Semma, the sone of Age, of Arari. And Filisteis weren gaderid in the stacioun; forsothe there was a feeld ful of lente; and whanne the puple fledde fro the face of Filisteis,
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 he stood in the myddis of the feeld, and bihelde it; and he smoot Filisteis, and the Lord made greet helthe.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 Also and thre men yeden doun bifore, that weren princes among thretti, and camen to Dauid in the tyme of reep in to the denne of Odollam. Forsothe the castels of Filisteis weren set in the valei of giauntis.
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 And Dauid was in a strong hold; sotheli the stacioun of Filisteis was thanne in Bethleem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 Therfor Dauid desiride water of the lake, and seide, If ony man wolde yyue to me drynk of watir of the cisterne, which is in Bethleem, bisidis the yate.
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 Therfor thre stronge men braken in to the castels of Filisteis, and drowen watir of the cisterne of Bethleem, that was bisidis the yate, and brouyten to Dauid; and he nolde drinke,
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 but offride it to the Lord, and seide, The Lord be merciful to me, that Y do not this; whether Y schal drynke the blood of these men, that yeden forth, and the perel of soulis? Therfor he nolde drynke. Thre strongeste men diden thes thingis.
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 Also Abisay, brother of Joab, the sone of Saruye, was prince of thre; he it is that reiside his schaft ayens thre hundrid men, whiche he killide; `he was nemid among thre,
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 and was the noblere among thre, and he was the prince of hem; but he cam not to the thre firste men.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 And Banaye, the sone of Joiada, strongeste man of grete werkis, of Capseel, he smoot twei liouns of Moab, `that is, twei knyytis hardi as liouns; and he yede doun, and smoot a lioun in the myddil cisterne in the daies of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 Also he killide a man of Egipt, a man worthi of spectacle, hauynge a spere in the hond; therfor whanne he hadde come doun with a yerde to that man, bi miyt he wrooth out the spere fro the hond of the man of Egipt, and killide hym with his owne spere.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 Banaye, sone of Joiada, dide these thingis;
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 and he was nemyed among thre stronge men, that weren among the thretti noblere men; netheles he cam not til to the thre. And Dauid made hym a counselour of priuyte to hym silf.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Asahel, the brother of Joab, was among thretti men; Eleanan, the sone of his fadris brother, of Bethleem; Semma, of Arari;
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Elcha, of Arodi; Helas, of Phelti;
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Hira, sone of Aches, of Thecua; Abiezer, of Amatoth;
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Mobannoy, of Cosathi; Selmon, of Achotes;
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Macharai, of Nethopath;
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heled, the sone of Baana, and he was of Netophath; Hiray, sone of Rabai, of Gebeeth, of the sones of Beniamyn; Banay, of Effrata;
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Hedday, of the stronde of Gaas;
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abiadon, of Arbath; Asmaneth, of Berromy;
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliaba, of Sabony; sones of Assen, Jonathan, and Jasan; Semma, of Herodi;
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Hayam, sone of Sarai, of Zaroth;
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelech, sone of Saalbai, the sone of Maachati; Heliam, sone of Achitofel, of Gilo;
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Esrai, of Carmele; Pharai, of Arbi;
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Ygaal, sone of Nathan, of Soba;
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Bonny, of Gaddi; Silech, of Ammony; Naarai, of Beroth, the squyer of Joab, the sone of Saruye;
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Haray, of Jethri; Gareb, and he was of Gethri;
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Vrye, of Ethei; alle weren seuene and thretti men.
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >