< 2 Samuel 12 >

1 Therfor the Lord sente Nathan to Dauid; and whanne he hadde come to Dauid, he seide to Dauid, Answere thou doom to me; twei men weren in o citee; o man was riche, and the tother was pore.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 The riche man hadde ful many scheep, and oxun;
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 sotheli the pore man hadde vttirli no thing, outakun o litil scheep, which he hadde bouyt, and nurschid, and which `hadde wexid at hym with hise sones, and eet togidere of his breed, and drank of his cuppe, and slepte in his bosum; and it was as a douyter to hym.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Forsothe whanne a pilgrym `hadde come to the riche man, he sparide to take of hise scheep and oxun, that he schulde make a feeste to that pilgrym, that cam to hym; and he took the scheep of the pore man, and `made redi metis to the man that cam to hym.
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Forsothe Dauid was ful wrooth with indignacioun ayens that man, and seide to Nathan, The Lord lyueth, for the man that dide this is the sone of deeth;
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 he schal yelde the scheep in to foure folde, for he dide this word, and sparide not.
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 Forsothe Nathan seide to Dauid, Thou art thilke man, that hast do this thing. The Lord God of Israel seith these thingis, Y anoyntide thee `in to kyng on Israel, and Y delyuerede thee fro the hond of Saul,
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 and Y yaf to thee the hows of thi lord, and the wyues of thi lord in thi bosum, and Y yaf to thee the hows of Israel, and of Juda; and if these thingis ben litil, Y schal adde to thee myche grettere thingis.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Whi therfor hast thou dispisid the word of the Lord, that thou didist yuels in my siyt? Thou hast smyte by swerd Vrye Ethei, and thou hast take his wijf in to wijf to thee, and thou hast slayn hym with the swerd of the sones of Amon.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Wherfor swerd schal not go awey fro thin hows til in to with outen ende; for thou dispysidist me, and tokist the wijf of Vrye Ethei, that sche schulde be thi wijf.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Therfor the Lord seith these thingis, Lo! Y schal reise on thee yuel of thin hows, and Y schal take thi wyues in `thin iyen, and Y schal yyue to thi neiybore, and he schal slepe with thi wyues in the iyen of this sunne, `that is, opynli bifor alle men, as in xv. chapitre.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 For thou hast do priueli; forsothe Y schal do this word in the siyt of al Israel, and in the siyt of this sunne.
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 And Dauid seide to Nathan, Y haue synned to the Lord. And Nathan seide to Dauid, Also the Lord hath turned awei thi synne; thou schalt not die.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Netheles for thou madist enemyes to blasfeme the name of the Lord, for this word the child which is borun to thee schal die bi deeth.
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 And Nathan turnede ayen in to his hows. And the Lord smoot the litil child, whom the wijf of Vrye childide to Dauid, and he dispeiride.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 And Dauid preiede the Lord for the litil child; and Dauid fastide bi fastyng, and entride asidis half, and lai on the erthe.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 Sotheli the eldere men of his hows camen, and constreyneden hym `bi meke preieris, that he schulde rise fro the erthe; and he nolde, nethir he eet mete with hem.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 Forsothe it bifelde in the seuenthe dai, that the yong child diede; and the seruauntis of Dauid dredde to telle to hym, that the litil child was deed; for thei seiden, Lo! whanne the litil child lyuede yit, we spaken to hym, and he herde not oure vois; hou myche more, if we seien the child is deed, he schal turment himsilf?
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 Therfore whanne Dauid hadde herd his seruauntis spekynge priueli, `ether moterynge, he understood that the yong child was deed; `and he seyde to his seruauntis, Whether the child is deed? Whiche answeriden to hym, He is deed.
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Therfor Dauid roos fro the erthe, and was waischid, and anoyntid; and whanne he hadde chaungid cloth, he entride in to the hows of the Lord, and worschipide, and cam in to his hows; and he axide, that thei schulden sette breed to hym, and he eet.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Sothely his seruauntis seiden to hym, What is the word which thou hast do? Thou fastidist, and weptist for the yong child, whanne he lyuede yit; sotheli whanne the child was deed, thou risidist and etist breed?
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 And Dauid seide, Y fastide and wepte for the yong child, whanne he lyuyde yit; for Y seide, Who woot, if perauenture the Lord yyue hym to me, and the yong child lyue?
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 `Now forsothe for he is deed, whi `fast Y? whether Y schal mow ayen clepe hym more? Y schal `go more to hym, but he schal not turne ayen to me.
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 And Dauid coumfortid Bersabee, his wijf; and he entride to hir, and slepte with hir. And sche gendride a sone, and Dauid clepide his name Salomon; and the Lord louyde hym.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 And he sente Salomon in the hond of Nathan, the prophete; and he clepide his name Amyable to the Lord, for the Lord louyde hym.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Therfor Joab fauyt ayens Rabath, of the sones of Amon, and he fauyt ayens the `kyngis citee.
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 And Joab sente messangeris to Dauid, and seide, Y fauyte ayens Rabath, and the citee of watris schal be takun.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Now therfor gadere thou the tother part of the puple, and bisege thou the citee, and take thou it, lest whanne the citee is wastid of me, the victorie be arettid to my name.
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 Therfor Dauid gaderide al the puple, and he yede forth ayens Rabath; and whanne he hadde fouyte, he took it.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 And he took the diademe of the kyng of hem fro his heed, bi weiyte a talent of gold, hauynge preciouseste peerlis; and it was put on the heed of Dauid, `that is, aftir that it was weldid and purgid bi fier; but also Dauid bar awey ful myche prey of the citee.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 Also he ledde forth the puple therof, and sawide, and `dide aboute hem `yrun instrumentis of turment, and departide with knyues, and `ledde ouer bi the licnesse of tijl stoonus; so he dide to alle the citees of the sones of Amon. And Dauid turnede ayen, and al his oost, in to Jerusalem.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Samuel 12 >