< 2 Samuel 11 >

1 Forsothe it was doon, whanne the yeer turnede ayen in that tyme wherynne kyngis ben wont to go forth to batels, Dauid sente Joab, and with hym hise seruauntis, and al Israel; and thei distrieden the sones of Amon, and bisegiden Rabath; forsothe Dauid dwellide in Jerusalem.
Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
2 While these thingis weren doon, it befelde, that Dauid roos in a dai fro his bed after mydday, and walkide in the soler of the kyngis hows; and he siy a womman waischynge hir silf euen ayens on hir soler; sotheli the womman was ful fair.
Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
3 Therfor the kyng sente, and enqueride, what womman it was; and it was teld to hym, that sche was Bersabee, the douytir of Heliam, and was the wijf of Vrye Ethei.
Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
4 Therfor bi messangeris sent Dauid took hir; and whanne sche entride to hym, he slepte with hir, and anoon sche was halewid fro hir vnclenesse.
Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
5 And sche turnede ayen in to hir hows, with child conseyued; and sche sente, and telde to Dauid, and seide, Y haue conseyued.
Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
6 Forsothe Dauid sente to Joab, and seide, Sende thou Vrye Ethei to me; and Joab sente Vrye to Dauid.
Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
7 And Vrie cam to Dauid; and Dauid axide, hou riytfuli Joab dide and the puple, and hou the batel was mynystrid.
Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
8 And Dauid seide to Vrye, Go in to thin hows, and waische thi feet. Vrye yede out fro the hows of the kyng, and the kyngis mete suede hym.
Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
9 Sotheli Vrye slepte bifor the yate of the kyngis hows with othere seruauntis of his lord, and yede not doun to his hows.
Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
10 And it was teld to Dauid of men, seiynge, Vrye `yede not to his hows. And Dauid seide to Vrye, Whether thou camest not fro the weye? whi yedist thou not doun in to thin hows?
Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
11 And Vrie seide to Dauid, The arke of God, Israel and Juda dwellen in tentis, and my lord Joab, and the seruauntis of my lord dwellen on the face of erthe, and schal Y go in to myn hows, to ete and drynke, and slepe with my wijf? Bi thin helthe, and bi the helthe of thi soule, Y schal not do this thing.
Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
12 Therfor Dauid seide to Vrye, Dwelle thou here also to dai, and to morewe Y schal delyuere thee. Vrie dwellide in Jerusalem in that day and the tothir.
Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
13 And Dauid clepide hym, that he schulde ete and drynke bifor hym, and Dauid made drunkun Vrye; and he yede out in the euentid, and slepte in his bed with the seruauntes of his lord; and yede not doun in to his hows.
Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
14 Therfor the morewtid was maad, and Dauid wroot epistle to Joab, and sente bi the hond of Vrye,
Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
15 and wroot in the pistle, Sette ye Vrye euene ayens the batel, where the batel is strongeste, `that is, where the aduersaries ben stronge, and forsake ye hym, that he be smitun and perische.
Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
16 Therfor whanne Joab bisegide the citee, he settide Vrie in the place where he wiste that strongeste men weren.
Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
17 And men yeden out of the citee, and fouyten ayens Joab, and thei killiden of the puple of seruauntis of Dauid, and also Vrye Ethei was deed.
Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
18 Therfor Joab sente, and telde alle the wordis of the batel;
Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
19 and he comaundyde to the messanger, and seide, Whanne thou hast fillid alle wordis of the batel to the kyng,
Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
20 if thou seest, that he is wrooth, and seith, Whi neiyiden ye to the wal to fiyte? whether ye wisten not, that many dartis ben sent `fro aboue fro the wal?
mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
21 who smoot Abymelech, sone of Gerobaal? whether not a womman sente on hym a gobet of a mylnestoon fro the wal, and killide hym in Thebes? whi neiyiden ye bisidis the wal? thou schalt seie, Also thi seruaunt, Vrye Ethei, diede.
Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
22 Therfor the messanger yede, and telde to Dauid alle thingis whiche Joab hadde comaundid to hym.
Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
23 And the messanger seide to Dauid, `Men hadden the maistri ayens us, and thei yeden out to vs in to the feeld; sotheli bi `fersnesse maad we pursueden hem `til to the yate of the citee.
Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
24 And archeris senten dartis to thi seruauntis fro the wal aboue, and summe of the `kyngis seruauntis ben deed; forsothe also thi seruaunt, Vrye Ethei, is deed.
Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
25 And Dauid seide to the messanger, Thou schalt seie these thingis to Joab, This thing breke not thee; for the bifallyng of batel is dyuerse, and swerd wastith now this man, now that man; coumforte thi fiyteris ayens the citee, that thou distrye it, and excite thou hem.
Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
26 Forsothe the wijf of Vrye herde, that Vrye hir hosebond was deed, and sche biweilide hym.
Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
27 And whanne the morenyng was passid, Dauid sente, and brouyte hir in to his hows; and sche was maad wijf to hym, and sche childide a sone to hym. And this word which Dauid hadde do displeside bifor the Lord.
Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.

< 2 Samuel 11 >