< 2 Chronicles 36 >

1 Therfor the puple of the lond took Joachaz, the sone of Josie, and ordeynede hym kyng for his fadir in Jerusalem.
Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
2 Joachaz was of thre and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede thre monethis in Jerusalem.
Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
3 Sotheli the kyng of Egipt, `whan he hadde come to Jerusalem, remouyde hym, and condempnede the lond in an hundrid talentis of siluer and in a talent of gold.
Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
4 And he ordeynede for hym Eliachim, his brother, kyng on Juda and Jerusalem; and turnede his name Joakym. Sotheli he took thilk Joachaz with hym silf, and brouyte in to Egipt.
Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
5 Joakym was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnyde eleuene yeer in Jerusalem, and he dide yuel bifor `his Lord God.
Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
6 Nabugodonosor, kyng of Caldeis, styede ayens this Joakym, and ledde hym boundun with chaynes in to Babiloyne.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
7 To which Babiloyne he translatide also the vessels of the Lord, and settide tho in his temple.
Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
8 Sotheli the residue of wordis of Joakym, and of hise abhomynaciouns whiche he wrouyte, and that weren foundun in hym, ben conteyned in the book of kyngis of Israel and of Juda. Therfor Joachym, his sone, regnede for hym.
Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Joachym was of eiyte yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede thre monethis and ten daies in Jerusalem, and he dide yuel in the siyt of the Lord.
Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
10 And whanne the cercle of the yeer was turned aboute, Nabugodonosor the kynge sente men, whiche also brouyten hym in to Babiloyne, whanne the moost preciouse vessels of the hows of the Lord weren borun out togidir. Sotheli he ordeynede Sedechie, his fadris brother, kyng on Juda and Jerusalem.
Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
11 Sedechie was of oon and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede eleuene yeer in Jerusalem.
Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
12 And he dide yuel in the siyt of `his Lord God, and he was not aschamed of the face of Jeremye, the prophete, spekynge to hym bi the mouth of the Lord.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
13 Also he yede awey fro the kyng Nabugodonosor, that hadde made hym to swere bi God; and he made hard his nol and herte, that he nolde turne ayen to the Lord of Israel.
Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
14 But also alle the princes of preestis and the puple trespassiden wickidli, bi alle abhomynaciouns of hethene men; and thei defouliden the hows of the Lord, which he halewide to hym silf in Jerusalem.
Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
15 Forsothe the Lord God of her fadris sente to hem bi the hond of hise messangeris, and roos bi nyyt, and amonestide ech day; for he sparide his puple and dwellyng place.
Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
16 And thei scorneden the messangeris of God, and dispisiden hise wordis, and scorneden hise prophetis; til the greet veniaunce of the Lord stiede on his puple, and noon heelyng were.
Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
17 And he brouyte on hem the kyng of Caldeis; and killide the yonge men of hem `bi swerd in the hows of seyntuarie; `he hadde not merci of a yong `man, and of a vergyn, and of an eld man, and sotheli nether of a man niy the deth for eldnesse, but he bitook alle in the hond of that king of Caldeis.
Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
18 And he translatide in to Babiloyne alle the vessels of the hows of the Lord, bothe the grettere and the lasse vessels, and the tresours of the temple, and of the kyng, and of the princes.
Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
19 Enemyes brenten the hows of the Lord; thei distrieden the wal of Jerusalem; thei brenten alle the touris; and thei distrieden what euer thing was preciouse.
Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
20 If ony man ascapide the swerd, he was led in to Babiloyne, and seruyde the kyng and hise sones; til the kyng of Peersis regnyde,
Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
21 and the word of the Lord bi the mouth of Jeremye was fillid, and til the lond halewide hise sabatis. For in alle the daies of desolacioun it made sabat, til that seuenti yeer weren fillid.
Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
22 Forsothe in the firste yeer of Cyrus, kyng of Persis, to fille the word of the Lord, which he hadde spoke bi the mouth of Jeremye, the Lord reiside the spirit of Cirus, king of Persis, that comaundide to be prechid in al his rewme, yhe, bi scripture, and seide, Cirus,
Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
23 the king of Persis, seith these thingis, The Lord God of heuene yaf to me alle the rewmes of erthe, and he comaundide to me, that Y schulde bilde to hym an hows in Jerusalem, which is in Judee. Who of you is in al his puple? `his Lord God be with hym, and stie he `in to Jerusalem.
Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”

< 2 Chronicles 36 >