< 2 Chronicles 26 >

1 Forsothe al the puple of Juda made kyng, Ozie, his sone, `of sixtene yeer, for his fader Amasie.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 He bildide Hailath, and restoride it to the lordschipe of Juda, after that the kyng slepte with hise fadris.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Ozie was of sixtene yeer, whanne he bigan to regne; and he regnede two and fifti yeer in Jerusalem; the name of his modir was Hiechelia, of Jerusalem.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 And he dide that, that was riytful in the siyt of the Lord, bi alle thingis whiche Amasie, his fadir, hadde do.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 And he souyte the Lord in the daies of Zacarie, vndurstondynge and seynge God; and whanne he souyte God, God reulide hym in alle thingis.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Forsothe he yede out, and fauyt ayens Filisteis, and distriede the wal of Geth, and the wal of Jabyne, and the wal of Azotus; and he bildide stronge places in Azotus and in Filistiym.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 And the Lord helpide hym bothe ayens Filisteis, and ayens Arabeis that dwelliden in Garbahal, and ayenus Amonytis.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 Amonytis paieden yiftis to Ozie, and his name was pupplischid `til to the entryng of Egipt for ofte victories.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 And Ozie bildide touris in Jerusalem ouer the yate of the corner, and ouer the yate of the valey, and othere touris in the same side of the wal; and made tho stidefast.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 Also he bildide touris in the wildirnesse, and he diggide ful many cisternes; for he hadde many beestis as wel in the feeldi places as in the wastnesse of deseert. Also he hadde vyneris and tiliers of vynes in the hilles, and in Carmele; for he was a man youun to erthetilthe.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Forsothe the oost of hise werriours, that yeden forth to batels, vndur the hond of Heiel, scribe, and of Masie, techere, and vndur the hond of Ananye that was of the duykis of the kyng;
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 and al the noumbre of princes, by her meynees, was of stronge men two thousynde and sixe hundrid.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 And vndur hem was al the oost, thre hundrid thousynde and seuen thousynde and fyue hundrid, that weren able to batel, and fouyten for the king ayens aduersaries.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 And Ozie made redi to hem, that is, to al the oost, scheldis, and speris, and basynetis, and haburiouns, and bouwis, and slyngis to caste stonys.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 And he made in Jerusalem engynes of dyuerse kynde, which he settide in touris, and in the corneris of wallis, that tho schulden caste arowis and grete stoonys; and his name yede out fer, for the Lord helpide hym, and hadde maad him strong.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 But whanne he was maad strong, his herte was reisid in to his perischyng; and he dispiside `his Lord God; and he entride in to the temple of the Lord, and wolde brenne encense on the auter of encense.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 And anoon Azarie, the preest, entride after hym, and with hym the preestis of the Lord, seuenti `men ful noble;
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 whiche ayenstoden the kyng, and seiden, Ozie, it is not of thin office, that thou brenne encense to the Lord, but of the preestis of the Lord, that is, of the sones of Aaron, that ben halewid to siche seruyce; go thou out of the seyntuarye; dispise thou not; for this thing schal not be arettid of the Lord God to thee in to glorie.
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 And Ozie was wrooth, and he helde in the hond the censere for to offre encence, and manaasside the preestis; and anoon lepre was sprungun forth in his forheed, bifor the preestis in the hows of the Lord on the auter of encense.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 And whanne Azarie, the bischop, hadde biholde hym, and alle othere preestis `hadden biholde him, thei sien lepre in his forheed, and hiyngli thei puttiden hym out; but also he was aferd, and hastide to go out; for he feelide anoon the veniaunce of the Lord.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 Therfor kyng Ozie was leprouse `til to the dai of his deeth, and dwellide in an hows bi it silf, and he was ful of lepre; `for which he was cast out of the hows of the Lord. Forsothe Joathan, his sone, gouernyde the hows of the kyng, and demyde the puple of the lond.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Sotheli Ysaie, the prophete, the sone of Amos, wroot the residue `of the formere and of the laste wordis of Ozie.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 And Ozie slepte with hise fadris, and thei birieden not hym in the feeld of the kyngis sepulcris, for he was leprouse; and Joathan, his sone, regnyde for hym.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 26 >