< 1 Samuel 8 >

1 Forsothe it was don, whanne Samuel hadde wexide eld, he settide hise sones iugis on Israel.
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 And the name of his firste gendrid sone was Johel, and the name of the secounde was Abia, iugis in Bersabee.
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 And hise sones yeden not in `the weies of hym, but thei bowiden after aueryce, and thei token yiftis, and peruertiden doom.
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 Therfor alle the grettere men in birthe of Israel weren gaderid, and camen to Samuel in to Ramatha.
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 And thei seiden to hym, Lo! thou hast wexid eld, and thi sones goen not in thi weies; ordeyne thou a kyng to vs, `that he deme vs, as also alle naciouns han.
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 And the word displeside in the iyen of Samuel, for thei hadden seid, Yyue thou to vs a kyng, that he deme vs. And Samuel preiede to the Lord.
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 Forsothe the Lord seide to Samuel, Here thou the vois of the puple in alle thingis whiche thei speken to thee; for thei han not caste awey thee, but me, that Y regne not on hem.
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 Bi alle her werkis whiche thei diden, fro the day in whiche Y ledde hem out of Egipt `til to this dai, as thei forsoken me, and seruyden alien goddis, so thei doon also to thee.
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 Now therfor here thou her vois; netheles witnesse thou to hem; biforseie thou to hem the riyt of the kyng, that schal regne on hem.
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 Therfor Samuel seide alle the wordis of the Lord to the puple, that hadde axid of him a king; and he seide,
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 This schal be the `riyt of the kyng, that schal comaunde to you; he schal take youre sones, and schal sette in hise charis;
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 and he schal make hem `to hym silf rideris, and biforegoeris of hise cartis; and he schal ordeyne to hym tribunes, `that is, souereyns of a thousynd, and centuriouns, `that is, souereyns of an hundrid, and eereris of hise feeldis, and reperis of cornes, and smythis of hise armeris, and charis.
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 Also he schal make youre douytris makeris of `oynementis to hym silf, and fueris, and bakeris.
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 And he schal take youre feeldis and vyneris and the beste places of olyues, and schal yyue to hise seruauntis.
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 But also he schal take the tenthe part of youre cornes, and rentis of vyneris, that he yyue to his chaumberleyns and seruauntis.
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 Sotheli he schal take awey youre seruauntis and handmaydes, and beste yong men, and assis, and schal sette in his werk.
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 Also he schal take the tenthe part of youre flockis, and ye schulen be `seruauntis to hym.
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 And ye schulen crye in that dai fro the face of youre kyng, whom ye han chose to you; and the Lord schal not here you in that dai; for ye axiden a kyng to you.
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 Sotheli the puple nolde here the vois of Samuel, but thei seiden, Nay for a kyng schal be on vs;
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 and we also schulen be as alle folkis, and oure kyng schal deme vs, and he schal go out bifor vs, and he schal fiyte oure batel for vs.
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 And Samuel herde alle the wordis of the puple, and `spak tho in the eeris of the Lord.
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 Forsothe the Lord seide to Samuel, Here thou `the vois of hem, and ordeyne thou a kyng on hem. And Samuel seide to the men of Israel, Ech man go in to his citee.
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

< 1 Samuel 8 >