< 1 Samuel 29 >

1 Therfor alle the cumpenyes of Filisteis weren gaderid in Aphec, but also Israel settide tentis aboue the welle that was in Jezrael.
Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
2 And sotheli the princis of Filisteis yeden in cumpenyes of an hundrid, and in thousyndis; forsothe Dauid and hise men weren in the laste cumpenye with Achis.
Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 And the princes of Filisteis seiden to Achis, What wolen these Ebreis to hem silf? And Achis seide to the princes of Filisteis, Whether ye knowen not Dauid, that was the seruaunt of Saul, kyng of Israel? and he was with me in many daies, `ether yeeris, and Y foond not in hym ony thing, fro the dai, in which he fledde to me `til to this dai.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
4 Sotheli the princes of Filisteis weren wrooth ayens hym, and seiden to hym, The man turne ayen, and sitte in his place, in which thou hast ordened hym, and come he not down with vs in to batel, lest he be maad aduersarie to vs, whanne we han bigunne to fiyte; for hou mai he plese his lord in other maner, no but in oure heedis?
Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
5 Whether this is not Dauid, to whom thei sungen in daunsis, and seiden, Saul smoot in thousyndis, and Dauid smoot in hise ten thousyndis?
Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
6 Therfor Achis clepide Dauid, and seide to hym, The Lord lyueth; for thou art riytful, and good in my siyt, and thi goyng out and `thin entryng is with me in castels, and Y `foond not in thee ony thing of yuel, fro the day in which thou camest to me til to this dai; but thou plesist not the princis.
Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
7 Therfor turne thou ayen, and go in pees, and offende thou not the iyen of princis of Filisteis.
Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
8 And Dauid seide to Achis, Forsothe what `dide Y, and what hast thou founde in me thi seruaunt, fro the dai in which Y was in thi siyt til in to this dai, that Y come not, and fiyte ayens the enemyes of my lord the kyng?
Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
9 Forsothe Achis answeride, and spak to Dauid, Y woot that thou art good, and as the aungel of God in my iyen; but the princes of Filisteis seyden, He schal not stie with vs in to batel.
Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
10 Therfor rise thou eerli, thou, and thi seruauntis that camen with thee; and whanne ye han ryse bi nyyt, and it bigynneth to be cleer, go ye.
Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
11 Therfor Dauid roos bi nyyt, he and hise men, that thei schulden go forth eerli, and turne ayen to the lond of Fylisteis; sotheli Filisteis stieden in to Jezrael.
Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

< 1 Samuel 29 >