< 1 Samuel 28 >

1 Forsothe it was doon in tho daies, Filisteis gaderiden her cumpenyes, that thei schulden be maad redi ayens Israel to batel. And Achis seide to Dauid, Thou witynge `wite now, for thou schalt go out with me in castels, thou and thi men.
Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
2 And Dauid seide to Achis, Now thou schalt wyte what thingis thi seruaunt schal do. And Achis seide to Dauid, And Y schal sette thee kepere of myn heed in alle dayes.
Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
3 Forsothe Samuel was deed, and al Israel biweilide hym, and thei birieden hym in Ramatha, his citee. And Saul dide awey fro the lond witchis and fals dyuynours, `and he slouy hem that hadden `charmers of deuelis `in her wombe.
Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
4 And Filisteis weren gaderid, and camen, and settiden tentis in Sunam; sotheli and Saul gaderide al Israel, and cam in to Gelboe.
Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
5 And Saul siy the castels of Filisteis, and he dredde, and his herte dredde greetli.
Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
6 And he counselide the Lord; and the Lord answeride not to hym, nether bi preestis, nether bi dremes, nether bi profetis.
Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
7 And Saul seide to hise seruauntis, Seke ye to me a womman hauynge a feend spekynge in the wombe; and Y schal go to hir, and Y schal axe bi hir. And hise seruauntis seiden to hym, A womman hauynge a feend spekynge in the wombe is in Endor.
Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
8 Therfor Saul chaungide his clothing, and he was clothid with othere clothis; and he yede, and twei men with hym; and thei camen to the womman in the nyyt. And he seyde, Dyuyne thou to me in a fend spekynge in the wombe, and reise thou to me whom Y schal seie to thee.
Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
9 And the womman seide to hym, Lo! thou woost hou grete thingis Saul hath do, and hou he dide awei fro the lond witchis, and fals dyuynours; whi therfor settist thou tresoun to my lijf, that Y be slayn?
Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
10 And Saul swoor to hir in the Lord, and seide, The Lord lyueth; for no thing of yuel schal come to thee for this thing.
Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
11 And the womman seide to hym, Whom schal Y reise to thee? And he seide, Reise thou Samuel to me.
Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
12 Sotheli whanne the womman hadde seyn Samuel, sche criede with greet vois, and seide to Saul, Whi hast thou disseyued me? for thou art Saul.
Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
13 And the kyng seide to hir, Nyl thou drede; what hast thou seyn? And the womman seide to Saul, Y siy goddis stiynge fro erthe.
Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
14 And Saul seide to hir, What maner forme is of hym? And sche seide, An eld man stieth, and he is clothid with a mentil. And Saul vndirstood that it was Samuel; and Saul bowide hym silf on his face to the erthe, and worschipide.
Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
15 Sotheli Samuel seide to Saul, Whi hast thou disesid me, that Y schulde be reisid? And Saul seide, Y am constreyned greetli; for Filisteis fiyten ayens me, and God yede awei fro me, and he nolde here me, nether bi the hond of profetis, nether bi dremes; therfor Y clepide thee, that thou schuldist schewe to me what Y schal do.
Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
16 And Samuel seide, What axist thou me, whanne God hath go awei fro thee, and passide to thin enemy?
Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
17 For the Lord schal do to thee as he spak in myn hond, and he schal kitte awey thi rewme fro thin hond, and he schal yyue it to Dauid, thi neiybore;
Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
18 for thou obeiedist not to the vois of the Lord, nether didist the `ire of hys strong veniaunce in Amalech. Therfor the Lord hath do to thee to day that that thou suffrist;
Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
19 and the Lord schal yyue also Israel with thee in the hond of Filisteis. Forsothe to morewe thou and thi sones schulen be with me; but also the Lord schal bitake the castels of Israel in the hond of Filistiym.
Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
20 And anoon Saul felde stretchid forth to erthe; for he dredde the wordis of Samuel, and strengthe was not in hym, for he hadde not ete breed in al that dai and al nyyt.
Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
21 Therfor thilke womman entride to Saul, and seide; for he was disturblid greetli; and sche seide to hym, Lo! thin handmayde obeiede to thi vois, and Y haue put my lijf in myn hond, and Y herde thi wordis, whiche thou spakist to me.
Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
22 Now therfor and thou here the vois of thin handmaide, and Y schal sette a mussel of breed bifor thee, and that thou etynge wexe strong, and maist do the iourney.
Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
23 And he forsook, and seide, Y schal not ete. Sothely hise seruauntis and the womman compelliden hym; and at the laste, whanne the vois of hem was herd, he roos fro the erthe, and sat on the bed.
Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
24 Sotheli thilke womman hadde a fat calf in the hows, and `sche hastide, and killide hym; and sche took mele, and meddlide it, and made therf breed;
Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
25 and settide bifor Saul and bifor hise seruauntis, and whanne thei hadden ete, thei risiden, and walkiden bi al that nyyt.
Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.

< 1 Samuel 28 >