< 1 Samuel 19 >

1 Forsothe Saul spak to Jonathas, his sone, and to alle hise seruauntis, that thei schulden sle Dauid; certis Jonathas, the sone of Saul, louyde Dauid greetli.
Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide.
2 And Jonathas schewide to Dauid, and seide, Saul, my fadir, sekith to sle thee, wherfor, Y biseche, kepe `thou thee eerli; and thou schalt dwelle priueli, and thou schalt be hid.
Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko.
3 Sotheli Y schal go out, and stonde bisidis my fadir in the feeld, where euer he schal be; and Y schal speke of thee to my fadir, and what euer thing Y shal se, Y schal telle to thee.
Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”
4 Therfor Jonathas spak good thingis of Dauid to Saul, his fadir, and seide to hym, Kyng, do thou not synne ayens thi seruaunt Dauid, for he `synnede not to thee, and hise werkis ben ful good to thee;
Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri.
5 and he puttide his lijf in his hond, and he killide the Filistei. And the Lord made greet heelthe to al Israel; thou siy, and were glad; whi therfor synnest thou in giltles blood, and sleest Dauid, which is with out gilt?
Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”
6 And whanne Saul hadde herd this, he was plesid with the vois of Jonathas, and swoor, `The Lord lyueth, `that is, bi the Lord lyuynge, for Dauid schal not be slayn.
Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”
7 Therfor Jonathas clepide Dauid, and schewide to hym alle these wordis. And Jonathas brouyte in Dauid to Saul, and he was bifor hym as `yistirdai and the thridde dai ago.
Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.
8 Forsothe batel was moued eft; and Dauyd yede out, and fauyt ayens Filisteis, and he smoot hem with a greet wounde, and thei fledden fro his face.
Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.
9 And the yuel spirit of the Lord was maad on Saul; sotheli he sat in his hows, and helde a spere; certis Dauid harpide in his hond.
Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze,
10 And Saul enforside to prene with the spere Dauid in the wal; and Dauid bowide fro `the face of Saul; forsothe the spere `with voide wounde was borun in to the wal; and Dauid fledde, and was saued in that niyt.
Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.
11 Therfor Saul sente hise knyytis in the nyyt in to the hows of Dauid, that thei schulden kepe hym, and that he `schulde be slayn in the morewtide. And whanne Mychol, the wijf of Dauid, hadde teld this to Dauid, and seide, If thou sauest not thee in this nyyt, thou schalt die to morew;
Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.”
12 sche puttide hym doun bi a wyndow. Forsothe he yede, and fledde, and was sauyd.
Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka.
13 Sotheli Mychol took an ymage, and puttide it on the bed, and puttide `an heeri skyn of geet at the heed therof, and hilide it with clothis.
Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.
14 Forsothe Saul sente sergeauntis, `that schulden rauysche Dauid, and it was answeride, that he was sijk.
Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”
15 And eft Saul sente messangeris, that thei schulden se Dauid, and he seide, Brynge ye hym to me in the bed, that he be slayn.
Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.”
16 And whanne the messangeris hadden come, `a symylacre was foundun on the bed, and `skynnes of geet at the heed therof.
Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.
17 And Saul seide to Mychol, Whi scornedist thou me so, and `delyueredist myn enemy, that he fledde? And Mychol answeride to Saul, For he spak to me, and seide, Delyuere thou me, ellis Y schal slee thee.
Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?” Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’”
18 Forsothe Dauid fledde, and was sauyd; and he cam to Samuel in to Ramatha, and telde to hym alle thingis which Saul hadde do to hym; and he and Samuel yeden, and dwelliden in Naioth.
Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti.
19 Forsothe it was teld to Saul of men, seiynge, Lo! Dauid is in Naioth in Ramatha.
Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.”
20 Therfor Saul sente sleeris, that thei schulden rauysche Dauid; and whanne thei hadden seyn the cumpeny of profetis profeciynge, and Samuel stondynge ouer hem, the Spirit of the Lord, `that is, the spirit of deuocioun, was maad in hem, and thei also bigunnen to prophecie.
Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera.
21 And whanne this was teld to Saul, he sente also othere messangeris; `sotheli and thei profesieden. And eft Saul sente the thridde messangeris, and thei prophecieden. And Saul was wrooth `with irefulnesse;
Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa.
22 and he also yede in to Ramatha, and he cam `til to the greet cisterne, which is in Socoth, and he axide, and seide, In what place ben Samuel and Dauid? And it was seid to hym, Lo! thei ben in Naioth in Ramatha.
Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?” Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”
23 And he yede in `to Naioth in Ramatha; and the Spirit of the Lord was maad also on him; and he `yede, and entride, and propheciede, `til the while he cam `in to Naioth in Ramatha.
Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti.
24 And `he also dispuylide him silf of hise clothis, and propheciede with othere men bifor Samuel, and he profeciede nakid in al that dai and nyyt. Wherfor `a prouerbe, that is, a comyn word, yede out, Whether and Saul among prophetis?
Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”

< 1 Samuel 19 >