< 1 Samuel 18 >

1 And it was doon, whanne Dauid `hadde endid to speke to Saul, the soule of Jonathas was glued togidre to the soule of Dauid, and Jonathas louyde hym as his owne soule.
Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
2 And Saul took Dauid in that dai, and grauntide not `to hym, `that he schulde turne ayen in to `the hows of his fadir.
Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
3 Forsothe Jonathas and Dauid maden boond of pees, `that is, swerynge euerlastynge frenschip; for Jonathas louyde Dauid as his owne soule;
Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
4 for whi Jonathas dispuylide him silf fro the coote `in which he was clothid, and yaf it to Dauid, and hise othere clothis, `til to his swerd and bouwe, and `til to the girdil.
Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
5 Also Dauid yede out to alle thingis, to what euer thingis Saul `hadde sent hym, and he gouernede hym silf prudentli; and Saul settide hym ouer the men of batel, and `he was acceptid, `ether plesaunt, in the iyen of al the puple, and moost in the siyt of `the seruauntis of Saul.
Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
6 Forsothe whanne Dauid turnede ayen, whanne `the Filistei was slayn, and bar the heed of `the Filistei in to Jerusalem, wymmen yeden out of alle the citees of Israel, and sungen, and ledden queris, ayens the comyng of king Saul, in tympans of gladnesse, and in trumpis.
Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
7 And the wymmen sungen, pleiynge, and seiynge, Saul smoot a thousynde, and Dauid smoot ten thousynde.
Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
8 Saul was wrooth greetli, and this word displeside `in his iyen; and he seide, Thei yauen ten thousynde to Dauid, and `thei yauen a thousynde to me; what leeueth to hym, no but the rewme aloone?
Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
9 Therfor Saul bihelde Dauid not with `riytful iyen, `fro that dai and afterward.
Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
10 Sotheli aftir the tother dai a wickid spirit of God asailide Saul, and he propheciede in the myddis of his hows.
Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
11 Forsothe Dauid harpide with his hond, as bi alle daies; and Saul helde a spere, and caste it, and gesside that he myyte prene Dauid with the wal, that is, perse with the spere, so that it schulde passe til to the wal; and Dauid bowide `fro his face the secounde tyme.
Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
12 And Saul dredde Dauid, for the Lord was with hym, and hadde go awei fro him silf.
Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
13 Therfor Saul remouide Dauid fro hym silf, and made hym tribune on a thousynde men; and Dauid yede out and entride in `the siyt of the puple.
Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
14 And Dauid dide warli in alle hise weies, and the Lord was with hym;
Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
15 and so Saul siy that Dauid was ful prudent, and he bigan to be war of Dauid.
Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
16 Forsothe al Israel and Juda louyden Dauid; for he entride and yede out bifor hem.
Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
17 And Saul seide to Dauid, Lo! `my more douytir Merob, Y schal yiue her wijf to thee; oneli be thou a strong man, and fiyte thou the `batels of the Lord. Forsothe Saul `arettide, and seide, Myn hond be not in hym, but the hond of Filisteis be on hym.
Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
18 Sotheli Dauid seide to Saul, Who am Y, ether what is my lijf, ether the meynee of my fadir in Israel, that Y be maad the `sone in lawe of the kyng?
Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
19 Forsothe the tyme `was maad whanne Merob, the douyter of Saul, `ouyte to be youun to Dauid, sche was youun wijf to Hadriel Molatite.
Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
20 Forsothe Dauid louide Mychol, the douytir of Saul; and it was teld to Saul, and it pleside hym.
Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
21 And Saul seide, Y schal yyue hir to hym, that it be to hym in to sclaundir, and the hond of Filisteis be on hym. Therfor Saul seide to Dauid, In `twei douytris thou schalt be my sone in lawe to dai.
Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
22 And Saul comaundide to hise seruauntis, Speke ye to Dauid, while it `is hid fro me, and seie ye, Lo! thou plesist the king, and alle hise seruauntis louen thee; now therfor be thou hosebonde of the `douytir of the kyng.
Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
23 And the seruauntis of Saul spaken alle these wordis in the eeris of Dauid. And Dauid seide, Whether it semeth litil to you `to be sone in lawe of the kyng? Forsothe Y am a pore man, and a feble.
Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
24 And the seruauntis telden to Saul, and seiden, Dauid spak siche wordis.
Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
25 Sotheli Saul seide, Thus speke ye to Dauid, The kyng hath no nede to yiftis for spowsails, no but onely to an hundrid prepucies, `that is, mennus yerdis vncircumcidid, `of Filisteis, that veniaunce be maad of the kyngis enemyes. Certis Saul thouyte to bitake Dauid in to the hondis of Filisteis.
Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
26 And whanne the seruauntis of Saul hadden teld to Dauid the wordis, whiche Saul hadde seid, the word pleside `in the iyen of Dauid, that he schulde be maad the kyngis son in lawe.
Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
27 And aftir a fewe daies Dauid roos, and yede in to Acharon, with the men that weren with hym, and he killide of Filisteis twei hundrid men; and brouyte `the prepucies of hem, and noumbride tho to the kyng, that he schulde be the kyngis sone in lawe. And so Saul yaf Mycol, his douyter, wiif to hym.
Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
28 And Saul siy, and vndirstood, that the Lord was with Dauid.
Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
29 Forsothe Mychol, `the douyter of Saul, louide Dauid, and Saul bigan more to drede Dauid; and Saul was maad enemye to Dauid in alle daies.
iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
30 And the princes of Filisteis yeden out; forsothe fro the bigynnyng of her goyng out Dauyd bar hym silf more warli than alle the men of Saul; and the name of Dauid was maad ful solempne.
Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.

< 1 Samuel 18 >