< 1 Kings 13 >

1 And lo! a man of God cam fro Juda, bi the word of the Lord, in to Bethel, while Jeroboam stood on the auter, `and castide encence.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 And `the man of God criede ayens the auter, bi the word of the Lord, and seide, Auter! auter! the Lord seith these thingis, Lo! a sone, Josias by name, shal be borun to the hows of Dauid; and he schal offre on thee the preestis of hiye thingis, that brennen now encensis yn thee, and he schal brenne the bonys of men on thee.
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 And he yaf a signe in that dai, `and seide, This schal be `the signe that the Lord spak, Lo! the auter schal be kit, and the aische which is `there ynne, schal be sched out.
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 And whanne the kyng hadde herd the word of the man of God, which word he hadde cried ayens the auter in Bethel, the kyng helde forth his hond fro the auter, and seide, Take ye hym. And his hond driede, which he hadde holde forth, and he myyte not drawe it ayen to hym silf.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 Also the auter was kit, and the aische was sched out of the auter, bi the signe which the man of God bifor seide, in the word of the Lord.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 And the kyng seide to the man of God, Biseche thou the face of thi Lord God, and preie thou for me, that myn hond be restorid to me. And the man of God preiede the face of God; and the hond of the king turnede ayen to hym, and it was maad as it was bifore.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 Sotheli the kyng spak to the man of God, Come thou hoom with me, that thou ete, and Y schal yyue yiftis to thee.
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 And the man of God seide to the kyng, Thouy thou schalt yyue to me the half part of thin hows, Y schal not come with thee, nether Y schal ete breed, nether Y schal drynke watir in this place;
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 `for so it is comaundid to me bi the word of the Lord, comaundinge, Thou schalt not ete breed, nether thou schalt drynke water, nether thou schalt turne ayen bi the weie bi which thou camest.
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 Therfor he yede bi another weie, and turnede not ayen bi the weie, bi which he cam in to Bethel.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 Forsothe sum elde profete dwellide in Bethel, to whom hise sones camen, and telden to hym alle the werkis whiche the man of God hadde do in that dai in Bethel; and thei telden to her fader the wordis whiche he spak to the kyng.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 And the fadir of hem seide to hem, Bi what weie yede he? Hise sones schewiden to hym the weie, bi which the man of God yede, that cam fro Juda.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 And he seide to hise sones, Sadle ye an asse to me. And whanne thei hadden sadlid,
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 he stiede, and yede after the man of God, and foond hym sittyng vndur a terebynte. And he seide to the man of God, Whether thou art the man of God, that camest fro Juda? He answeride, Y am.
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 And he seide to hym, Come thou with me hoom, that thou ete breed.
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 And he seide, Y may not turne ayen, nether come with thee, nether Y schal ete breed, nether Y schal drynke water in this place;
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 for the Lord spak to me in the word of the Lord, and seide, Thou schalt not ete breed, and thou schalt not drynke water there, nether thou schalt turne ayen bi the weie bi which thou yedist.
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 Which seide to hym, And Y am a profete lijk thee; and an aungel spak to me bi the word of the Lord, and seide, Lede ayen hym in to thin hows, that he ete breed, and drynke watir. He disseyuede the man of God,
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 and brouyte him ayen with hym. Therfor he ete breed in his hows, and drank watir.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 And whanne he sat at the table, the word of the Lord was maad to the prophete that brouyte hym ayen;
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 and he criede to the man of God that cam fro Juda, and seide, The Lord seith these thingis, For thou obeidist not to the mouth of the Lord, and keptist not the comaundement which thi Lord God comaundide to thee,
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 and thou turnedist ayen, and etist breed, and drankist watir in the place in which Y comaundide to thee, that thou schuldist not ete breed, nether schuldist drynke watir, thi deed bodi schal not be borun in to the sepulcre of thi fadris.
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 And whanne he hadde ete and drunke, the prophete, whom he hadde brouyt ayen, sadlide his asse.
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 And whanne he hadde go, a lioun foond hym in the weye, and killide hym. And his deed bodi was cast forth in the weie; sotheli the asse stood bisydis hym, and the lioun stood bisidis the deed bodi.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 And lo! men passynge sien the deed bodi cast forth in the weye, and the lyoun stondynge bisidis the deed bodi; and thei camen, and pupplischiden in the citee, in which thilke eeld prophete dwellide.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 And whanne thilke prophete, that brouyte hym ayen fro the weye, hadde herd this, he seide, It is the man of God, that was vnobedient to the mouth of God; and the Lord bitook hym to the lioun, that brak hym, and killide hym, bi the word of the Lord which he spak to hym.
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 And he seide to hise sones, Sadle ye an asse to me.
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 And whanne thei hadden sadlid, and he hadde go, he foond his deed bodi cast forth in the weie, and the asse and the lioun stondinge bisidis the deed bodi; and the lioun eet not the deed bodi, nether hirtide the asse.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 Therfor the profete took the deed bodi of the man of God, and puttide it on the asse; and he turnede ayen, and brouyte it in to the cyte of the eeld prophete, that he schulde biweile hym.
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 And he puttide his deed bodi in his sepulcre, and thei biweiliden him, Alas! alas! my brother!
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 And whanne thei hadden biweilid hym, he seide to hise sones, Whanne Y schal be deed, birie ye me in the sepulcre, in which the man of God is biried; putte ye my bonys bisidis hise bonys.
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 For sotheli the word schal come, which he bifor seide in the word of the Lord, ayens the auter which is in Bethel, and ayens alle the templis of hiy placis, that ben in the citees of Samarie.
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 After these wordis Jeroboam turnede not ayen fro his werste weie, but ayenward of the laste puplis he made preestis of hiye places; who euer wolde, fillide his hond, and he was maad preest of hiy placis.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 And for this cause the hows of Jeroboam synnede, and it was distried, and doon awey fro the face of erthe.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< 1 Kings 13 >