< 1 Corinthians 8 >
1 But of these thingis that ben sacrified to ydols, we witen, for alle we han kunnyng. But kunnyng blowith, charite edefieth.
Tsopano za chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano: Ife tidziwa kuti tonse tili ndi chidziwitso. Komatu chidziwitso chokha chimadzitukumula, koma chikondi ndicho chimapindulitsa.
2 But if ony man gessith, that he kan ony thing, he hath not yit knowe hou it bihoueth hym to kunne.
Munthu amene amaganiza kuti amadziwa kanthu, ndiye kuti sakudziwa monga mmene amayenera kudziwira.
3 And if ony man loueth God, this is knowun of hym.
Koma munthu amene amakonda Mulungu amadziwika ndi Mulunguyo.
4 But of metis that ben offrid to idols, we witen, that an idol is no thing in the world, and that ther is no God but oon.
Choncho kunena za chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano; ife tikudziwa kuti mafano si kanthu nʼpangʼonongʼono pomwe pa dziko lapansi, ndiponso kuti palibe Mulungu wina koma mmodzi yekha.
5 For thouy ther ben summe that ben seid goddis, ethir in heuene, ether in erthe, as ther ben many goddis, and many lordis;
Popeza kuti ngakhale pali yotchedwa milungu, kaya ndi kumwamba kapena pa dziko lapansi (poti ilipodi milungu yambirimbiri ndi ambuye ambirimbiri),
6 netheles to vs is o God, the fadir, of whom ben alle thingis, and we in hym; and o Lord Jhesu Crist, bi whom ben alle thingis, and we bi hym.
koma kwa ife pali Mulungu mmodzi yekha, Atate, zinthu zonse zinachokera mwa Iye ndipo ndife ake. Komanso pali Ambuye mmodzi Yesu Khristu kumene zinthu zonse zinachokera ndipo mwa Iye ife tili ndi moyo.
7 But not in alle men is kunnyng. For summen with conscience of ydol til now eten as thing offrid to idolis; and her conscience is defoulid, for it is sijk.
Koma saliyense amadziwa zimenezi. Alipo ena ozolowera mafano kwambiri mwakuti akadya chakudya chotere amaganiza kuti chakudyacho chinaperekedwa nsembe kwa mafano. Ndiye poti chikumbumtima chawo nʼchofowoka chimadetsedwadi.
8 Mete comendith vs not to God; for nether we schulen faile, if we eten not, nether if we eten, we schulen haue plente.
Koma chakudya sichitisendeza kufupi ndi Mulungu. Tikapanda kudya si vuto, tikadya sitisinthikanso.
9 But se ye, lest perauenture this your leeue be maad hurtyng to sijke men.
Komabe samalani kuti ufulu wanu ochita zinthu usafike pokhumudwitsa ofowoka.
10 For if ony man schal se hym, that hath kunnyng, etynge in a place where idols ben worschipid, whethir his conscience, sithen it is sijke, schal not be edified to ete thingis offrid to idols?
Pakuti ngati aliyense wachikumbumtima chofowoka akakuonani achidziwitsonu mukudya mʼnyumba yopembedzera mafano, kodi iyeyo sichidzamulimbitsa mtima kuti azidya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano?
11 And the sijk brothir, for whom Crist diede, schal perische in thi kunnyng.
Kotero kuti chifukwa cha chidziwitso chanu mʼbale wofowokayu amene chifukwa cha iye, Khristu anafa, wawonongeka chifukwa cha chidziwitso chanu.
12 For thus ye synnyng ayens britheren, and smytynge her sijk conscience synnen ayens Crist.
Mukamachimwira abale anu motere ndikuwawonongera chikumbumtima chawo chofowokacho, mukuchimwira Khristu.
13 Wherfor if mete sclaundrith my brother, Y schal neuere ete fleisch, lest Y sclaundre my brothir. (aiōn )
Nʼchifukwa chake ngati zimene ine ndimadya zichititsa mʼbale wanga kugwa mu tchimo, sindidzadyanso chakudyacho kuti mʼbaleyo ndisamuchimwitse. (aiōn )