< 1 Chronicles 27 >

1 Forsothe the sones of Israel bi her noumbre, the princes of meynees, the tribunes, and centuriouns, and prefectis, that mynystriden to the kyng bi her cumpenyes, entrynge and goynge out bi ech monethe in the yeer, weren souereyns, ech bi hym silf, on foure and twenti thousynde.
Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
2 Isiboam, the sone of Zabdihel, was souereyn of the firste cumpenye in the firste monethe, and vndur hym weren foure and twenti thousynde;
Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
3 of the sones of Fares was the prince of alle princes in the oost, in the firste monethe.
Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
4 Dudi Achoites hadde the cumpany of the secounde monethe, and aftir hym silf he hadde another man, Macelloth bi name, that gouernede a part of the oost of foure and twenti thousynde.
Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
5 And Bananye, the sone of Joiada, the preest, was duyk of the thridde cumpenye in the thridde monethe, and four and twenti thousynde in his departyng;
Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
6 thilke is Bananye, the strongest among thritti, and aboue thritti; forsothe Amyzadath, his sone, was souereyn of his cumpenye.
Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
7 In the fourthe monethe, the fourthe prince was Asahel, the brother of Joab, and Zabadie, his sone, aftir hym, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
8 In the fifthe monethe, the fifthe prince was Samoth Jezarites, and foure and twenti thousynde in his cumpenye.
Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
9 In the sixte monethe, the sixte prince was Ira, the sone of Actes, Techuytes, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
10 In the seuenthe monethe, the seuenthe prince was Helles Phallonites, of the sones of Effraym, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
11 In the eiythe monethe, the eiythe prince was Sobothai Assothites, of the generacioun of Zarai, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
12 In the nynthe monethe, the nynthe prince was Abiezer Anathotites, of the generacioun of Gemyny, and foure and tweynti thousynde in his cumpeny.
Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
13 In the tenthe monethe, the tenthe prince was Maray, and he was Neophatites, of the generacioun of Zaray, and foure and twenti thousynde in his cumpany.
Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
14 In the elleuenthe monethe, the elleuenthe prince was Banaas Pharonytes, of the sones of Effraym, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
15 In the tweluethe monethe, the tweluethe prince was Holdia Nethophatites, of the generacioun of Gothonyel, and foure and twenti thousynde in his cumpeny.
Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
16 Forsothe these weren souereyns of the lynages of Israel; duyk Eliezer, sone of Zechri, was souereyn to Rubenytis; duyk Saphacie, sone of Maacha, was souereyn to Symeonytis;
Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
17 Asabie, the sone of Chamuel, was souereyn to Leuytis; Sadoch `was souereyn to Aaronytis;
mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
18 Elyu, the brothir of Dauid, `was souereyn to the lynage of Juda; Amry, the sone of Mychael, `was souereyn to Isacharitis;
mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
19 Jesmaye, the sone of Abdie, was souereyn to Zabulonytis; Jerymuth, the sone of Oziel, `was souereyn to Neptalitis;
mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
20 Ozee, the sone of Ozazym, `was souereyn to the sones of Effraym; Johel, the sone of Phatae, was souereyn to the half lynage of Manasses;
mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
21 and Jaddo, the sone of Zacarie, `was souereyn to the half lynage of Manasses in Galaad; sotheli Jasihel, the sone of Abner, `was souereyn to Beniamyn; forsothe Ezriel,
mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
22 the sone of Jeroam, was souereyn to Dan; these weren the princes of the sones of Israel.
mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
23 Forsothe Dauid nolde noumbre hem with ynne twenti yeer, for the Lord seide, that he wolde multiplie Israel as the sterris of heuene.
Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
24 Joab, the sone of Saruye, bigan for to noumbre, and he fillide not; for ire fel on Israel for this thing, and therfor the noumbre of hem, that weren noumbrid, was not teld in to the bookis of cronyclis of kyng Dauid.
Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
25 Forsothe Azymoth, the sone of Adihel, was on the tresouris of the kyng; but Jonathan, the sone of Ozie, was souereyn of these tresours, that weren in cytees, and in townes, and in touris.
Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
26 Sotheli Ezri, the sone of Chelub, was souereyn on the werk of hosebondrie, and on erthe tiliers, that tiliden the lond;
Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
27 and Semeye Ramathites was souereyn on tilieris of vyneris; sotheli Zabdie Aphonytes was souereyn on the wyn celeris;
Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
28 for Balanam Gadaritis was on the olyue placis, and fige places, that weren in the feeldi places; sotheli Joas was on the schoppis, `ether celeris, of oile;
Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
29 forsothe Cethray Saronytis `was souereyn of the droues, that weren lesewid in Sarena; and Saphat, the sone of Abdi, was ouer the oxis in valeys;
Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
30 sotheli Vbil of Ismael was ouer the camelis; and Jadye Meronathites was ouer the assis; and Jazir Aggarene was ouer the scheep;
Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
31 alle these weren princes of the catel of kyng Dauid.
Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
32 Forsothe Jonathas, brother of `Dauithis fader, was a councelour, a myyti man, and prudent, and lettrid; he and Jahiel, the sone of Achamony, weren with the sones of the kyng.
Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
33 Also Achitofel was a counselour of the kyng; and Chusi Arachites was a frend of the kyng.
Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
34 Aftir Achitofel was Joiada, the sone of Banaye, and Abyathar; but Joab was prince of the oost of the kyng.
Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

< 1 Chronicles 27 >