< 1 Chronicles 22 >

1 And Dauid seide, This is the hows of God, and this auter is in to brent sacrifice of Israel.
Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
2 And he comaundide that alle conuersis fro hethenesse to the lawe of Israel `schulden be gaderid `of the lond of Israel; and he ordeynede of hem masouns for to kytte stoonys and for to polische, that the hows of the Lord schulde be bildid;
Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
3 also Dauid made redy ful myche yrun to the nailes of the yatis, and to the medlyngis and ioyntouris, and vnnoumbrable weiyte of bras;
Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
4 also the trees of cedre myyten not be gessid, whiche the men of Sidonye and the men of Tyre brouyten to Dauid.
Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
5 And Dauid seide, Salomon, my sone, is a litil child and delicat; sotheli the hows, which Y wole be bildid to the Lord, owith to be sich, that it be named in alle cuntrees; therfor Y schal make redi necessaries to hym. And for this cause Dauid bifor his deeth made redi alle costis.
Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
6 And he clepide Salomon, his sone, and comaundide to hym, that he schulde bilde an hows to the Lord God of Israel.
Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
7 And Dauid seide to Salomon, My sone, it was my wille to bilde an hows to the name of `my Lord God;
Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
8 but the word of the Lord was made to me, and seide, Thou hast sched out myche blood, and thou hast fouyt ful many batels; thou mayst not bilde an hows to my name, for thou hast sched out so myche blood bifor me;
Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
9 the sone that schal be borun to thee, schal be a man most pesible, for Y schal make hym to haue reste of alle hise enemyes bi cumpas, and for this cause he schal be clepid pesible, and Y schal yyue pees and reste in Israel in alle hise daies.
Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
10 He schal bilde an hows to my name; he schal be to me in to a sone, and Y schal be to hym in to a fadir, and Y schal make stidefast the seete of his rewme on Israel withouten ende.
Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
11 Now therfor, my sone, the Lord be with thee, and haue thou prosperite, and bilde thou an hows to `thi Lord God, as he spak of thee.
“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
12 And the Lord yyue to thee prudence and wit, that thou mow gouerne Israel, and kepe the lawe of `thi Lord God.
Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
13 For thanne thou maist profite, if thou kepist the comaundementis and domes, whiche the Lord comaundide to Moises, that he schulde teche Israel; be thou coumfortid, and do manli, drede thou not `with outforth, nether drede thou `with ynne.
Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
14 Lo! in my pouert Y haue maad redi the costis of the hows of the Lord; an hundrid thousinde talentis of gold, and a thousynde thousynde talentis of siluer; sotheli of bras and irun is no weiyte, for the noumbre is ouercomun bi greetnesse; Y haue maad redi trees and stoonys to alle costis.
“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
15 Also thou hast ful many crafti men, masouns, and leggeris of stonys, and crafti men of trees, and of alle craftis,
Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
16 most prudent to make werk, in gold, and siluer, and bras, and in yrun, of which is no noumbre; therfor rise thou, and make, and the Lord schal be with thee.
zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
17 Also Dauid comaundide to alle the princis of Israel, that thei schulden helpe Salomon,
Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
18 his sone, and seide, Ye seen, that `youre Lord God is with you, and hath youe to you reste `by cumpas, and hath bitake alle enemyes in youre hoond, and the erthe is suget bifor the Lord, and bifor his puple.
Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
19 Therfor yyue youre hertis and youre soulis, that ye seke `youre Lord God; and rise ye togidere, and bilde ye a seyntuarie to `youre Lord God, that the arke of boond of pees of the Lord be brouyt in, and that vessels halewid to the Lord be brouyt in to the hows, which is bildid to the name of the Lord.
Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

< 1 Chronicles 22 >