< 1 Chronicles 11 >

1 Therfor al Israel was gaderid to Dauid in Ebron, and seide, We ben thi boon and thi fleisch;
Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
2 also yisterdai and the thridde dai ago, whanne Saul regnede yit on Israel, thou it were that leddist out and leddist in Israel; for `thi Lord God seide to thee, Thou schalt fede my puple Israel, and thou schalt be prince on it.
Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
3 Therfor alle the gretter in birthe of Israel camen to the kyng in Ebron; and Dauid maad with hem a boond of pees bifor the Lord, and thei anoyntiden hym kyng on Israel, bi the word of the Lord, which he spak in the hond of Samuel.
Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
4 Therfor Dauid yede, and al Israel, in to Jerusalem; this Jerusalem is Jebus, where Jebuseis enhabiteris of the lond weren.
Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
5 And thei that dwelliden at Jebus seiden to Dauid, Thou schalt not entre hidur. Forsothe Dauid took the hiy tour of Syon, which is the citee of Dauid;
anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
6 and he seide, Ech man that `sleeth first Jebusei, schal be prince and duyk. Therfor Joab, sone of Saruye, stiede first, and was maad prince.
Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
7 Sotheli Dauid dwellide in the hiy tour, and therfor it was clepid the cytee of Dauid;
Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
8 and he bildide the citee in cumpas fro Mello til to the cumpas; forsothe Joab bildide the tother part of the citee.
Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
9 And Dauid profitide goynge and wexynge, and the Lord of oostis was with hym.
Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
10 These ben the princes of the stronge men of Dauid, that helpiden hym, that he schulde be kyng on al Israel, bi the word of the Lord which he spak to Israel.
Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
11 And this is the noumbre of the stronge men of Dauid; Jesbaam, the sone of Achamony, was prince among thretti; this reiside his schaft ethir spere on thre hundrid woundid men in o tyme.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
12 And after hym was Eleazar, the sone of his fadris brothir, and was `a man of Ahoit, which Eleazar was among thre miyti men.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
13 This was with Dauid in Aphesdomyn, whanne Filisteis weren gaderid to o place in to batel; and a feeld of that cuntrey was ful of barli, and the puple fledde fro the face of Filisteis.
Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
14 This Eleazar stood in the myddis of the feeld, and defendide it; and whanne he hadde slayn Filisteis, the Lord yaf greet helthe to his puple.
Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
15 Sotheli thre of thritti princes yeden doun to the stoon, wher ynne Dauid was, to the denne of Odolla, whanne Filisteis settiden tentis in the valey of Raphaym.
Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
16 Forsothe Dauid was in a strong hold, and the stacioun, `that is, the oost gaderid, of Filisteis was in Bethleem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
17 Therfor Dauid desiride watir, and seide, Y wolde, that sum man yaf to me water of the cisterne of Bethleem, which is in the yate.
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
18 Therfor these thre yeden thoruy the myddil of the castelis of Filisteis, and drowen watir of the cisterne of Bethleem, that was in the yate, and thei brouyten to Dauid, that he schulde drynke; and Dauid nolde `drynke it, but rather he offride it to the Lord, and seide, Fer be it,
Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
19 that Y do this thing in the siyt of my God, and that Y drynke the blood of these men, for in the perel of her lyues thei brouyten watir to me; and for this cause he nolde drynke. Thre strongeste men diden these thingis.
Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
20 Also Abisai, the brother of Joab, he was the prince of thre men, and he reiside his schaft ayens thre hundrid woundid men; and he was moost named among thre,
Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
21 among the secounde thre he was noble, and the prince of hem; netheles he cam not til to the firste thre.
Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
22 Banaye, the sone of Joiada, strongest man of Capsael, that dide many werkis; he killide two stronge men of Moab; and he yede doun, and killide a lioun in the myddil of a cisterne, in the tyme of snow;
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
23 and he killide a man of Egipt, whos stature was of fyue cubitis, and he hadde a spere as the beem of webbis; therfor Banaye yede doun to hym with a yerde, and rauyschide the spere, which he held in the hond, and killide hym with his owne spere.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
24 Banaye, the sone of Joiada, dide these thingis, that was moost named among thre stronge men, and was the firste among thretti;
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
25 netheles he cam not til to the thre; sotheli Dauid settide hym at his eere.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
26 Forsothe the strongeste men `in the oost weren Asael, the brother of Joab, and Eleanan, the sone of his fadris brothir of Bethleem,
Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27 Semynoth Arorites, Helles Phallonytes, Iras,
Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
28 the sone of Acces of Thecue, Abieser of Anathot,
Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
29 Sobochay Sochites, Ylai Achoytes,
Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
30 Maray Nethophatithes, Heles, the sone of Banaa, Nethophatithes, Ethaa,
Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
31 the sone of Rabai, of Gabaath of the sones of Beniamyn; Banaye Pharatonythes, men of the stronde Gaas,
Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32 Abihel Arabatithes, Azmoth Baruanythes, Eliaba Salaonythes,
Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
33 the sones of Assem Gesonythes, Jonathan, the sone of Saga, Ararithes, Achiam,
Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
34 the sone of Achar, Ararites,
ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35 Eliphal, the sone of Mapher,
Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
36 Mechoratithes, Ahya Phellonythes,
Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
37 Asrahi Carmelites, Neoray,
Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
38 the sone of Thasbi, Johel, the brother of Nathan, Mabar, the sone of Aggaray, Selech Ammonythes,
Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
39 Nooray Berothites, the squyer of Joab, sone of Saruye,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
40 Iras Jetreus, Gareb Jethreus,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
41 Vrie Ethei, Sabab,
Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
42 the sone of Ooli, Adyna, the sone of Segar Rubenytes, prince of Rubenytis, and thritti men with hym;
Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
43 Hanan, the sone of Macha, and Josaphath Mathanythes, Ozias Astarothites,
Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
44 Semma and Jahel, the sones of Hotayn Aroerites,
Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
45 Ledihel, the sone of Zamri, and Joha, his brother, Thosaythes,
Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
46 Hehiel Maanytes, Jerybay and Josia, the sones of Helnaen, Jethma Moabites,
Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
47 Heliel, and Obed, and Jasihel of Masobia.
Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.

< 1 Chronicles 11 >