< Acts 1 >
1 The former treatise, O Theophilus, I made concerning all that Jesus undertook both to do and to teach;
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 till the day in which He was taken up, after He had by the holy Spirit given instructions to the apostles whom He had chosen:
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 to whom also He presented Himself alive, after He had suffered, by many certain proofs; being seen among them for forty days, and speaking of the things relating to the kingdom of God.
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 And meeting them together He commanded them not to depart from Jerusalem, but to wait for the promise of the Father, which, said He, ye have heard from me;
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 for John indeed baptized with water, but ye shall within a few days be baptized with the holy Spirit.
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Being therefore come together they asked Him, saying, Lord, wilt thou at this time restore the kingdom to Israel?
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 And He said unto them, It is not for you to know the times or seasons, which the Father hath reserved in his own power.
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 But ye shall receive power from the holy Spirit coming upon you: and ye shall be my witnesses both in Jerusalem, and in all Judea, and Samaria, and to the uttermost part of the earth.
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 And having said these things, as they were looking upon Him, He was lifted up, and a cloud received Him out of their sight.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 And while they were looking stedfastly toward heaven, as He went up, behold two men in white stood by them;
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 who said, Ye men of Galilee, why do ye stand gazing up to heaven? This Jesus who is taken up from you into heaven, shall so come in the manner ye have seen Him going into heaven.
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Then they returned to Jerusalem from the mountain called Olivet, which is from Jerusalem a sabbath-day's journey.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 And when they were come in to the city, they went up into an upper room, where Peter, and James, and John, and Andrew, Philip and Thomas, Bartholomew, and Matthew, James the son of Alpheus, and Simon the zealot, and Jude the brother of James, usually abode.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 These all persevered with one accord in prayer and supplication with the women, and Mary the mother of Jesus, and his brethren.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 And in these days Peter stood up in the midst of the disciples, (now the number of the persons that were together was about an hundred and twenty, )
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 and said, Men and brethren, it was necessary that this scripture should be fulfilled, which the holy Ghost spake by the mouth of David, concerning Judas, who was guide to them that apprehended Jesus:
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 for he was numbered with us, and had obtained a part of this ministry.
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 (Now this man purchased a field with the reward of iniquity; and falling down on his face, burst asunder in the middle, and all his bowels gushed out:
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 (and it was known to all the inhabitants of Jerusalem, so that the field is called in their own dialect, Aceldama, that is, the field of blood: )
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 for it is written in the book of Psalms, Let his habitation be desolate, and let none dwell in it; and again, Let another take his office.)
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 Wherefore it is necessary that one of these men, who have been conversant with us all the time that the Lord Jesus came in and out among us,
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 from the baptism of John, till the day that He was taken up from us, should be joined with us as a witness of his resurrection.
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 And they proposed two, Joseph called Barsabas, who was surnamed Justus, and Matthias.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 And they prayed and said, Thou, Lord, who knowest the hearts of all, shew us, which of these two Thou hast chosen,
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 to take part of this ministry and apostleship, from which Judas is fallen by his transgression, that he might go to his own place.
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 And they gave out their lots, and the lot fell upon Matthias, and he was numbered with the apostles.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.