< Psalms 118 >

1 Give thanks to the LORD, for he is good, for his loving kindness endures forever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Let Israel now say that his loving kindness endures forever.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Let the house of Aaron now say that his loving kindness endures forever.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Now let those who fear the LORD say that his loving kindness endures forever.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Out of my distress, I called on the LORD. The LORD answered me with freedom.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 The LORD is on my side. I will not be afraid. What can man do to me?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 The LORD is on my side among those who help me. Therefore I will look in triumph at those who hate me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is better to take refuge in the LORD, than to put confidence in man.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is better to take refuge in the LORD, than to put confidence in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All the nations surrounded me, but in the LORD’s name I cut them off.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They surrounded me, yes, they surrounded me. In the LORD’s name I indeed cut them off.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They surrounded me like bees. They are quenched like the burning thorns. In the LORD’s name I cut them off.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 You pushed me back hard, to make me fall, but the LORD helped me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 The LORD is my strength and song. He has become my salvation [yeshu`ah].
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The voice of rejoicing and salvation [yeshu`ah] is in the tents of the righteous. “The right hand of the LORD does valiantly.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of the LORD is exalted! The right hand of the LORD does valiantly!”
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I will not die, but live, and declare the LORD’s works.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 The LORD has punished me severely, but he has not given me over to death.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open to me the gates of righteousness. I will enter into them. I will give thanks to the LORD.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This is the gate of the LORD; the righteous will enter into it.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I will give thanks to you, for you have answered me, and have become my salvation [yeshu`ah].
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 The stone which the builders rejected has become the cornerstone.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This is the LORD’s doing. It is marvelous in our eyes.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the day that the LORD has made. We will rejoice and be glad in it!
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Save us now, we beg you, LORD! LORD, we beg you, send prosperity now.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed is he who comes in the LORD’s name! We have blessed you out of the LORD’s house.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 The LORD is God, and he has given us light. Bind the sacrifice with cords, even to the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 You are my God, and I will give thanks to you. You are my God, I will exalt you.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Oh give thanks to the LORD, for he is good, for his loving kindness endures forever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalms 118 >