< Acts 8 >

1 Saul was consenting to his death. A great persecution arose against the assembly which was in Jerusalem in that day. They were all scattered abroad throughout the regions of Judea and Samaria, except for the emissaries.
Ndipo Saulo anavomerezana nawo pa imfa ya Stefano. Tsiku lomwelo, mpingo wa mu Yerusalemu unayamba kuzunzidwa, ndipo onse, kupatulapo atumwi, anabalalikira ku madera onse a Yudeya ndi Samariya.
2 Devout men buried Stephen and lamented greatly over him.
Anthu okonda Mulungu anayika maliro a Stefano ndipo anamulira kwambiri.
3 But Saul ravaged the assembly, entering into every house and dragged both men and women off to prison.
Koma Saulo anayamba kuwononga mpingo. Amapita nyumba ndi nyumba, ndipo amagwira amuna ndi amayi ndi kukawatsekera ku ndende.
4 Therefore those who were scattered abroad went around proclaiming the word.
Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita.
5 Philip went down to the city of Samaria and proclaimed to them the Messiah.
Filipo anapita ku mzinda wa ku Samariya ndipo analalikira za Khristu kumeneko.
6 The multitudes listened with one accord to the things that were spoken by Philip when they heard and saw the signs which he did.
Gulu la anthu litamva Filipo akulalikira komanso kuona zizindikiro zozizwitsa zimene ankazichita, onse anamvetsetsa zimene iye amanena.
7 For unclean spirits came out of many of those who had them. They came out, crying with a loud voice. Many who had been paralysed and lame were healed.
Mizimu yoyipa inatuluka mwa anthu ambiri ikufuwula kwambiri ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo ndi olumala anachiritsidwa.
8 There was great joy in that city.
Kotero munali chimwemwe chachikulu mu mzindawo.
9 But there was a certain man, Simon by name, who used to practise sorcery in the city and amazed the people of Samaria, making himself out to be some great one,
Koma mu mzindawo munali munthu dzina lake Simoni, amene amachita za matsenga ndi kudabwitsa anthu a mu Samariya. Iye amadzitamandira kuti ndi wopambana,
10 to whom they all listened, from the least to the greatest, saying, “This man is that great power of God.”
ndipo anthu onse, aakulu ndi aangʼono anamumvera ndi kunena kuti, “Munthu uyu ndi mphamvu ya Mulungu yotchedwa Mphamvu yayikulu.”
11 They listened to him because for a long time he had amazed them with his sorceries.
Anthu amamutsata chifukwa kwa nthawi yayitali amawadabwitsa ndi matsenga akewo.
12 But when they believed Philip proclaiming good news concerning God’s Kingdom and the name of Yeshua the Messiah, they were immersed, both men and women.
Koma atakhulupirira Filipo akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ndiponso dzina la Yesu Khristu, anthuwo anabatizidwa amuna ndi amayi.
13 Simon himself also believed. Being immersed, he continued with Philip. Seeing signs and great miracles occurring, he was amazed.
Nayenso Simoni anakhulupirira ndipo anabatizidwa, natsatira Filipo kulikonse, ndipo anadabwa kwambiri pamene anaona zizindikiro zazikulu ndi zozizwitsa.
14 Now when the emissaries who were at Jerusalem heard that Samaria had received the word of God, they sent Peter and Yochanan to them,
Atumwi a ku Yerusalemu atamva kuti anthu a ku Samariya analandira Mawu a Mulungu, anatumiza Petro ndi Yohane.
15 who, when they had come down, prayed for them, that they might receive the Holy Spirit;
Atafika anawapempherera kuti alandire Mzimu Woyera,
16 for as yet he had fallen on none of them. They had only been immersed in the name of Messiah Yeshua.
chifukwa Mzimu Woyera anali asanafike pa wina aliyense wa iwo; anali atangobatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
17 Then they laid their hands on them, and they received the Holy Spirit.
Ndipo Petro ndi Yohane anasanjika manja awo pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.
18 Now when Simon saw that the Holy Spirit was given through the laying on of the emissaries’ hands, he offered them money,
Simoni ataona kuti Mzimu anaperekedwa kwa iwo atumwi atawasanjika manja, iye anafuna kuwapatsa ndalama ndipo anati,
19 saying, “Give me also this power, that whomever I lay my hands on may receive the Holy Spirit.”
“Inenso ndipatseni mphamvu imeneyi kuti aliyense amene ndimusanjika manja anga azilandira Mzimu Woyera.”
20 But Peter said to him, “May your silver perish with you, because you thought you could obtain the gift of God with money!
Petro anayankha kuti, “Ndalama zako utayike nazo pamodzi, chifukwa unaganiza kuti ungathe kugula mphatso ya Mulungu ndi ndalama!
21 You have neither part nor lot in this matter, for your heart isn’t right before God.
Ulibe gawo kapena mbali pa utumikiwu, chifukwa mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu.
22 Repent therefore of this, your wickedness, and ask God if perhaps the thought of your heart may be forgiven you.
Lapa zoyipa zakozi ndipo upemphere kwa Ambuye. Mwina adzakukhululukira maganizo a mu mtima mwako.
23 For I see that you are in the poison of bitterness and in the bondage of iniquity.”
Pakuti ine ndikuona kuti ndiwe wowawidwa mtima ndiponso kapolo wa tchimo.”
24 Simon answered, “Pray for me to the Lord, that none of the things which you have spoken happen to me.”
Ndipo Simoni anayankha, “Mundipempherere kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.”
25 They therefore, when they had testified and spoken the word of the Lord, returned to Jerusalem, and preached the Good News to many villages of the Samaritans.
Atatha kuchitira umboni ndi kulalikira mawu a Ambuye, Petro ndi Yohane anabwerera ku Yerusalemu, atalalikira Uthenga Wabwino mʼmidzi yambiri ya Asamariya.
26 Then an angel of the Lord spoke to Philip, saying, “Arise, and go towards the south to the way that goes down from Jerusalem to Gaza. This is a desert.”
Mngelo wa Ambuye anati kwa Filipo, “Nyamuka pita chakummwera, ku msewu wa ku chipululu wopita ku Gaza kuchokera ku Yerusalemu.”
27 He arose and went; and behold, there was a man of Ethiopia, a eunuch of great authority under Candace, queen of the Ethiopians, who was over all her treasure, who had come to Jerusalem to worship.
Ndipo ananyamuka napita, ndipo akuyenda anakumana ndi munthu wa ku Etiopia wa udindo waukulu woyangʼanira chuma cha Kandake, mfumu yayikazi ya ku Etiopia. Munthu ameneyu anapita ku Yerusalemu kukapembedza Mulungu,
28 He was returning and sitting in his chariot, and was reading the prophet Isaiah.
ndipo akubwerera kwawo atakwera pa galeta lake amawerenga buku la mneneri Yesaya.
29 The Spirit said to Philip, “Go near, and join yourself to this chariot.”
Mzimu anamuwuza Filipo kuti, “Pita pa galeta ilo ndipo ukakhale pafupi nalo.”
30 Philip ran to him, and heard him reading Isaiah the prophet, and said, “Do you understand what you are reading?”
Pamenepo Filipo anathamangira ku galeta ndipo anamva munthuyo akuwerenga buku la mneneri Yesaya. Filipo anamufunsa kuti, “Kodi mukumvetsa zimene mukuwerengazi?”
31 He said, “How can I, unless someone explains it to me?” He begged Philip to come up and sit with him.
Iye anayankha kuti, “Ndingamvetse bwanji popanda wina wondimasulira?” Ndipo iye anayitana Filipo kuti abwere ndikukhala naye mʼgaleta.
32 Now the passage of the Scripture which he was reading was this, “He was led as a sheep to the slaughter. As a lamb before his shearer is silent, so he doesn’t open his mouth.
Mawu amene ndunayo imawerenga anali awa: “Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
33 In his humiliation, his judgement was taken away. Who will declare His generation? For his life is taken from the earth.”
Iye ananyozedwa ndipo panalibe chilungamo pa mlandu wake. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?”
34 The eunuch answered Philip, “Who is the prophet talking about? About himself, or about someone else?”
Ndunayo inamufunsa Filipo kuti, “Chonde, uzeni, kodi mneneri akuyankhula za ndani, za iye mwini kapena za munthu wina?”
35 Philip opened his mouth, and beginning from this Scripture, preached to him about Yeshua.
Pamenepo Filipo anayambira pa malemba omwewo kumuwuza za Uthenga Wabwino wa Yesu.
36 As they went on the way, they came to some water; and the eunuch said, “Behold, here is water. What is keeping me from being immersed?”
Akuyenda mu msewu anafika pamalo pamene panali madzi ndipo ndunayo inati, “Taonani madzi awa. Kodi pali chondiletsa kuti ndibatizidwe?”
Filipo anati, “Ngati mukhulupirira ndi mtima wanu wonse mukhoza kubatizidwa.” Ndunayo inayankha kuti, “Ine ndikukhulupirira kuti Yesu Khristu ndi Mwana wa Mulungu.”
38 He commanded the chariot to stand still, and they both went down into the water, both Philip and the eunuch, and he immersed him.
Ndipo analamulira galeta kuti liyime. Onse awiriwo, Filipo ndi Ndunayo anatsika ndi kulowa mʼmadzi ndipo Filipo anamubatiza.
39 When they came up out of the water, the Spirit of the Lord caught Philip away, and the eunuch didn’t see him any more, for he went on his way rejoicing.
Pamene iwo anatuluka mʼmadzimo, Mzimu wa Ambuye anamukwatula Filipo, ndipo Ndunayo sinamuonenso, koma inapitiriza ulendo wake ikusangalala.
40 But Philip was found at Azotus. Passing through, he preached the Good News to all the cities until he came to Caesarea.
Koma Filipo anapezeka kuti ali ku Azoto ndipo anazungulira konse, kulalikira Uthenga Wabwino mʼmizinda yonse mpaka anakafika ku Kaisareya.

< Acts 8 >