< Romans 3 >
1 Then what advantage does the Jew have? Or what is the profit of circumcision?
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Much in every way! Because first of all, they were entrusted with the revelations of God.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 For what if some were without faith? Will their lack of faith nullify the faithfulness of God?
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 May it never be! Yes, let God be found true, but every man a liar. As it is written, “that you might be justified in your words, and might prevail when you come into judgment.”
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 But if our unrighteousness commends the righteousness of God, what will we say? Is God unrighteous who inflicts wrath? I speak like men do.
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 May it never be! For then how will God judge the world?
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 For if the truth of God through my lie abounded to his glory, why am I also still judged as a sinner?
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 Why not (as we are slanderously reported, and as some affirm that we say), “Let’s do evil, that good may come?” Those who say so are justly condemned.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 What then? Are we better than they? No, in no way. For we previously warned both Jews and Greeks that they are all under sin.
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 As it is written, “There is no one righteous; no, not one.
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 There is no one who understands. There is no one who seeks after God.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 They have all turned away. They have together become unprofitable. There is no one who does good, no, not so much as one.”
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 “Their throat is an open tomb. With their tongues they have used deceit.” “The poison of vipers is under their lips.”
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 “Their mouth is full of cursing and bitterness.”
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 “Their feet are swift to shed blood.
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Destruction and misery are in their ways.
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 The way of peace, they haven’t known.”
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 “There is no fear of God before their eyes.”
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Now we know that whatever things the law says, it speaks to those who are under the law, that every mouth may be closed, and all the world may be brought under the judgment of God.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 Because by the works of the law, no flesh will be justified in his sight; for through the law comes the knowledge of sin.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 But now apart from the law, a righteousness of God has been revealed, being testified by the law and the prophets;
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 even the righteousness of God through faith in Jesus Christ to all and on all those who believe. For there is no distinction,
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 for all have sinned, and fall short of the glory of God;
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 being justified freely by his grace through the redemption that is in Christ Jesus,
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 whom God sent to be an atoning sacrifice through faith in his blood, for a demonstration of his righteousness through the passing over of prior sins, in God’s forbearance;
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 to demonstrate his righteousness at this present time, that he might himself be just and the justifier of him who has faith in Jesus.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Where then is the boasting? It is excluded. By what kind of law? Of works? No, but by a law of faith.
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 We maintain therefore that a man is justified by faith apart from the works of the law.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 Or is God the God of Jews only? Isn’t he the God of Gentiles also? Yes, of Gentiles also,
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 since indeed there is one God who will justify the circumcised by faith and the uncircumcised through faith.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Do we then nullify the law through faith? May it never be! No, we establish the law.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.