< Proverbs 3 >

1 My son, don’t forget my teaching, but let your heart keep my commandments,
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 for they will add to you length of days, years of life, and peace.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Don’t let kindness and truth forsake you. Bind them around your neck. Write them on the tablet of your heart.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 So you will find favor, and good understanding in the sight of God and man.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Trust in Yahweh with all your heart, and don’t lean on your own understanding.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 In all your ways acknowledge him, and he will make your paths straight.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Don’t be wise in your own eyes. Fear Yahweh, and depart from evil.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 It will be health to your body, and nourishment to your bones.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honor Yahweh with your substance, with the first fruits of all your increase;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 so your barns will be filled with plenty, and your vats will overflow with new wine.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 My son, don’t despise Yahweh’s discipline, neither be weary of his correction;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 for whom Yahweh loves, he corrects, even as a father reproves the son in whom he delights.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Happy is the man who finds wisdom, the man who gets understanding.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 For her good profit is better than getting silver, and her return is better than fine gold.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 She is more precious than rubies. None of the things you can desire are to be compared to her.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Length of days is in her right hand. In her left hand are riches and honor.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Her ways are ways of pleasantness. All her paths are peace.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 She is a tree of life to those who lay hold of her. Happy is everyone who retains her.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 By wisdom Yahweh founded the earth. By understanding, he established the heavens.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 By his knowledge, the depths were broken up, and the skies drop down the dew.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 My son, let them not depart from your eyes. Keep sound wisdom and discretion,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 so they will be life to your soul, and grace for your neck.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Then you shall walk in your way securely. Your foot won’t stumble.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 When you lie down, you will not be afraid. Yes, you will lie down, and your sleep will be sweet.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Don’t be afraid of sudden fear, neither of the desolation of the wicked, when it comes;
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 for Yahweh will be your confidence, and will keep your foot from being taken.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Don’t withhold good from those to whom it is due, when it is in the power of your hand to do it.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Don’t say to your neighbor, “Go, and come again; tomorrow I will give it to you,” when you have it by you.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Don’t devise evil against your neighbor, since he dwells securely by you.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Don’t strive with a man without cause, if he has done you no harm.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Don’t envy the man of violence. Choose none of his ways.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For the perverse is an abomination to Yahweh, but his friendship is with the upright.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Yahweh’s curse is in the house of the wicked, but he blesses the habitation of the righteous.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Surely he mocks the mockers, but he gives grace to the humble.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 The wise will inherit glory, but shame will be the promotion of fools.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbs 3 >