< Romans 5 >
1 Standing then acquitted as the result of faith, let us enjoy peace with God through our Lord Jesus Christ,
Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
2 through whom also, as the result of faith, we have obtained an introduction into that state of favour with God in which we stand, and we exult in hope of some day sharing in God's glory.
Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.
3 And not only so: we also exult in our sufferings, knowing as we do, that suffering produces fortitude;
Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira.
4 fortitude, ripeness of character; and ripeness of character, hope;
Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo.
5 and that this hope never disappoints, because God's love for us floods our hearts through the Holy Spirit who has been given to us.
Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
6 For already, while we were still helpless, Christ at the right moment died for the ungodly.
Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe.
7 Why, it is scarcely conceivable that any one would die for a simply just man, although for a good and lovable man perhaps some one, here and there, will have the courage even to lay down his life.
Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera.
8 But God gives proof of His love to us in Christ's dying for us while we were still sinners.
Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
9 If therefore we have now been pronounced free from guilt through His blood, much more shall we be delivered from God's anger through Him.
Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu.
10 For if while we were hostile to God we were reconciled to Him through the death of His Son, it is still more certain that now that we are reconciled, we shall obtain salvation through Christ's life.
Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye?
11 And not only so, but we also exult in God through our Lord Jesus Christ, through whom we have now obtained that reconciliation.
Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
12 What follows? This comparison. Through one man sin entered into the world, and through sin death, and so death passed to all mankind in turn, in that all sinned.
Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa.
13 For prior to the Law sin was already in the world; only it is not entered in the account against us when no Law exists.
Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo.
14 Yet Death reigned as king from Adam to Moses even over those who had not sinned, as Adam did, against Law. And in Adam we have a type of Him whose coming was still future.
Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
15 But God's free gift immeasurably outweighs the transgression. For if through the transgression of the one individual the mass of mankind have died, infinitely greater is the generosity with which God's grace, and the gift given in His grace which found expression in the one man Jesus Christ, have been bestowed on the mass of mankind.
Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri!
16 And it is not with the gift as it was with the results of one individual's sin; for the judgement which one individual provoked resulted in condemnation, whereas the free gift after a multitude of transgressions results in acquittal.
Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa.
17 For if, through the transgression of the one individual, Death made use of the one individual to seize the sovereignty, all the more shall those who receive God's overflowing grace and gift of righteousness reign as kings in Life through the one individual, Jesus Christ.
Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
18 It follows then that just as the result of a single transgression is a condemnation which extends to the whole race, so also the result of a single decree of righteousness is a life-giving acquittal which extends to the whole race.
Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo.
19 For as through the disobedience of the one individual the mass of mankind were constituted sinners, so also through the obedience of the One the mass of mankind will be constituted righteous.
Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
20 Now Law was brought in later on, so that transgression might increase. But where sin increased, grace has overflowed;
Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa.
21 in order that as sin has exercised kingly sway in inflicting death, so grace, too, may exercise kingly sway in bestowing a righteousness which results in the Life of the Ages through Jesus Christ our Lord. (aiōnios )
Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios )