< Luke 5 >

1 On one occasion the crowd was pressing on Him and listening to God's Message, while He was standing by the Lake of Gennesaret.
Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
2 He, however, saw two fishing-boats drawn up on the beach (for the men had gone away from them and were washing the nets),
Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
3 and going on board one of them, which was Simon's He asked him to push out a little from land. Then He sat down and taught the crowd of people from the boat.
Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
4 When He had finished speaking, He said to Simon, "Push out into deep water, and let down your nets for a haul."
Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
5 "Rabbi," replied Peter, "all night long we have worked hard and caught nothing; but at your command I will let down the nets."
Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
6 This they did, and enclosed a vast number of fish; and their nets began to break.
Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
7 So they signalled to their partners in the other boat to come and help them; they came, and they filled both the boats so that they almost sank.
Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
8 When Simon Peter saw this, he fell down at the knees of Jesus, and exclaimed, "Master, leave my boat, for I am a sinful man."
Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
9 (For he was astonished and terrified--he and all his companions--at the haul of fish which they had taken;
Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
10 and so were Simon's partners James and John, the sons of Zabdi.) But Jesus replied to Simon, "Fear not: from this time you shall be a catcher of men."
chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
11 Then, after bringing their boats to land, they left everything and followed Him.
Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
12 On another occasion, when He was in one of the towns, there was a man there covered with leprosy, who, seeing Jesus, threw himself at His feet and implored Him, saying, "Sir, if only you are willing, you are able to make me clean."
Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
13 Reaching out His hand and touching him, Jesus said, "I am willing; be cleansed!" And instantly the leprosy left him.
Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
14 He ordered him to tell no one. "But go," He said, "show yourself to the Priest, and make the offering for your purification which Moses appointed, as evidence for them."
Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
15 But all the more the report about Him spread abroad, and great multitudes crowded to hear Him and to be cured of their diseases;
Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
16 but Jesus Himself constantly withdrew into the Desert and there prayed.
Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
17 One day He was teaching, and there were Pharisees and teachers of the Law sitting there who had come from every village in Galilee and Judaea and from Jerusalem. And the power of the Lord was present for Him to cure people.
Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
18 And a party of men came carrying a palsied man on a bed, and they endeavoured to bring him in and lay him before Jesus.
Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
19 But when they could find no way of doing so because of the crowd, they went up on the roof and let him down through the tiling--bed and all--into the midst, in front of Jesus.
Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
20 He saw their faith and said to him, "Friend, your sins are forgiven."
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
21 Then the Scribes and Pharisees began to cavil, asking, "Who is this, uttering blasphemies? Who but God alone can forgive sins?"
Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
22 Well aware of their reasonings, Jesus answered their questions by asking in turn, "What is this that you are debating in your hearts?
Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
23 Which is easier? --to say, 'Your sins are forgiven,' or to say, 'Rise and walk'?
Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
24 But to prove to you that the Son of Man has authority on earth to forgive sins" --Turning to the paralytic He said, "I bid you, Rise, take up your bed, and go home."
Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
25 Instantly he stood up in their presence, took up the mattress on which he had been lying, and went away to his home, giving glory to God.
Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
26 Amazement seized them all. "Glory to God!" was the abiding feeling. Yet fear flashed through their minds and they said, "We have seen strange things to-day."
Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
27 After this He went out and noticed a tax-gatherer, Levi by name, sitting at the Toll office; and He said to him, "Follow me."
Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
28 He rose, left everything, and followed Him.
Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
29 Levi also gave a great entertainment at his house in honour of Jesus, and there was a large party of tax-gatherers and others at table with them.
Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
30 This led the Pharisees and Scribes of their party to expostulate with His disciples and ask, "Why are you eating and drinking with these tax-gatherers and notorious sinners?"
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
31 But Jesus replied to them, "It is not men in good health who require a physician, but the sick.
Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
32 I have not come to call the righteous to repentance, but sinners."
Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
33 Again they said to Him, "John's disciples fast often and pray, as do also those of the pharisees; but yours eat and drink."
Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
34 "Can you compel the bridal party to fast," replied Jesus, "so long as they have the bridegroom among them?
Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
35 But a time for this will come, when the Bridegroom has been taken away from them: then, at that time, they will fast."
Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
36 He also spoke in figurative language to them. "No one," He said, "tears a piece from a new garment to mend an old one. Otherwise he would not only spoil the new, but the patch from the new would not match the old.
Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
37 Nor does any one pour new wine into old wine-skins. Otherwise the new wine would burst the skins, the wine itself would be spilt, and the skins be destroyed.
Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
38 But new wine must be put into fresh wineskins.
Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
39 Nor does any one after drinking old wine wish for new; for he says, 'The old is better.'"
Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”

< Luke 5 >