< Romans 3 >
1 What advantage then hath the Jew? or what profit [is there] of circumcision?
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Much every way: chiefly, because that to them were committed the oracles of God.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 For what if some did not believe? will their unbelief make the faith of God without effect?
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 By no means: verily let God be true, but every man a liar; as it is written, That thou mayest be justified in thy sayings, and mayest overcome when thou art judged.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 But if our unrighteousness commendeth the righteousness of God, what shall we say? [Is] God unrighteous who taketh vengeance? (I speak as a man.)
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 By no means: for then how shall God judge the world?
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 For if the truth of God hath more abounded through my lie to his glory; why yet am I also judged as a sinner?
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 And not [rather] (as we are slanderously reported, and as some affirm that we say) Let us do evil, that good may come? whose damnation is just.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 What then? are we better [than they]? No, in no wise: for we have before proved both Jews and Gentiles, that they are all under sin;
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 As it is written, There is none righteous, no, not one:
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 There is none that understandeth, there is none that seeketh God.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 They are all gone out of the way, they are together become unprofitable: there is none that doeth good, no, not one.
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 Their throat [is] an open sepulcher; with their tongues they have used deceit; the poison of asps [is] under their lips:
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 Whose mouth [is] full of cursing and bitterness.
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 Their feet [are] swift to shed blood.
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Destruction and misery [are] in their ways:
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 And the way of peace have they not known.
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 There is no fear of God before their eyes.
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Now we know that whatever things the law saith, it saith to them who are under the law: that every mouth may be stopped, and all the world may become guilty before God.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 Therefore by the deeds of the law, there shall no flesh be justified in his sight: for by the law [is] the knowledge of sin.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 But now the righteousness of God without the law is manifested, being testified by the law and the prophets;
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 Even the righteousness of God, [which is] by faith of Jesus Christ to all, and upon all them that believe; for there is no difference:
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 For all have sinned, and come short of the glory of God;
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 Being justified freely by his grace, through the redemption that is in Jesus Christ:
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 Whom God hath set forth [to be] a propitiation, through faith in his blood, to declare his righteousness for the remission of sins that are past, through the forbearance of God;
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 To declare, [I say], at this time his righteousness: that he may be just, and the justifier of him who believeth in Jesus.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Where [is] boasting then? It is excluded. By what law? of works? No; but by the law of faith.
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 Therefore we conclude, that a man is justified by faith without the deeds of the law.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 [Is he] the God of the Jews only? [is he] not also of the Gentiles? Yes, of the Gentiles also:
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 Seeing [it is] one God who will justify the circumcision by faith, and uncircumcision through faith.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Do we then make void the law through faith? By no means: but we establish the law.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.