< Psalms 97 >
1 The LORD reigneth; let the earth rejoice; let the multitude of isles be glad.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Clouds and darkness surround him: righteousness and judgment [are] the habitation of his throne.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 A fire goeth before him, and burneth up his enemies round about.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 His lightnings enlightened the world: the earth saw, and trembled.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 The hills melted like wax at the presence of the LORD, at the presence of the LORD of the whole earth.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 The heavens declare his righteousness, and all the people see his glory.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Confounded be all they that serve graven images, that boast themselves of idols; worship him, all [ye] gods.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Zion heard, and was glad; and the daughters of Judah rejoiced because of thy judgments, O LORD.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 For thou, LORD, [art] high above all the earth: thou art exalted far above all gods.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Ye that love the LORD, hate evil: he preserveth the souls of his saints; he delivereth them out of the hand of the wicked.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Light is sown for the righteous, and gladness for the upright in heart.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Rejoice in the LORD, ye righteous; and give thanks at the remembrance of his holiness.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.