< Psalms 80 >
1 To the chief Musician upon Shoshannim Eduth, A Psalm of Asaph. Give ear, O Shepherd of Israel, thou that leadest Joseph like a flock; thou that dwellest [between] the cherubim, shine forth.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Before Ephraim and Benjamin and Manasseh stir up thy strength, and come [and] save us.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 Turn us again, O God, and cause thy face to shine; and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 O LORD God of hosts, how long wilt thou be angry against the prayer of thy people?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Thou feedest them with the bread of tears; and givest them tears to drink in great measure.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Thou makest us a strife to our neighbors: and our enemies laugh among themselves.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 Turn us again, O God of hosts, and cause thy face to shine; and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 Thou hast brought a vine out of Egypt: thou hast cast out the heathen, and planted it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 Thou preparedst [room] before it, and didst cause it to take deep root, and it filled the land.
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 The hills were covered with the shade of it, and its boughs [were like] the goodly cedars.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 She sent out her boughs to the sea, and her branches to the river.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Why hast thou [then] broke down her hedges, so that all they who pass by the way do pluck her?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 The boar from the wood doth waste it, and the wild beast of the field doth devour it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Return, we beseech thee, O God of hosts: look down from heaven, and behold, and visit this vine;
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 And the vineyard which thy right hand planted, and the branch [that] thou madest strong for thyself.
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 [It is] burnt with fire, [it is] cut down: they perish at the rebuke of thy countenance.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Let thy hand be upon the man of thy right hand, upon the son of man [whom] thou madest strong for thyself.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 So will we not go back from thee: revive us, and we will call upon thy name.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Turn us again, O LORD God of hosts, cause thy face to shine; and we shall be saved.
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.