< Psalms 60 >

1 To the chief Musician upon Shushan-eduth, Michtam of David, to teach; when he strove with Aram-naharaim and with Aram-zobah, when Joab returned, and smote of Edom in the valley of salt twelve thousand. O God, thou hast cast us off, thou hast scattered us, thou hast been displeased; O turn thyself to us again.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Thou hast made the earth to tremble; thou hast broken it: heal its breaches; for it shaketh.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Thou hast shown thy people hard things: thou hast made us to drink the wine of astonishment.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Thou hast given a banner to them that fear thee, that it may be displayed because of the truth. (Selah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 That thy beloved may be delivered; save [with] thy right hand, and hear me.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 God hath spoken in his holiness; I will rejoice, I will divide Shechem, and measure out the valley of Succoth.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Gilead [is] mine, and Manasseh [is] mine; Ephraim also [is] the strength of my head; Judah [is] my lawgiver;
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab [is] my washpot; over Edom will I cast out my shoe: Philistia, triumph thou because of me.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Who will bring me [into] the strong city? who will lead me into Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 [Wilt] thou not, O God, [who] hadst cast us off? and [thou], O God, [who] didst not go out with our armies?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Give us help from trouble: for vain [is] the help of man.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Through God we shall do valiantly: for he will tread down our enemies.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psalms 60 >