< Psalms 47 >
1 To the chief Musician, A Psalm for the sons of Korah. O clap your hands, all ye people; shout to God with the voice of triumph.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 For the LORD most high [is] terrible; [he is] a great King over all the earth.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 He shall subdue the people under us, and the nations under our feet.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 He shall choose our inheritance for us, the excellence of Jacob whom he loved. (Selah)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 God is gone up with a shout, the LORD with the sound of a trumpet.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Sing praises to God, sing praises: sing praises to our King, sing praises.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 For God [is] the King of all the earth: sing ye praises with understanding.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 God reigneth over the heathen: God sitteth upon the throne of his holiness.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 The princes of the people are assembled, [even] the people of the God of Abraham: for the shields of the earth [belong] to God: he is greatly exalted.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.