< Psalms 114 >

1 When Israel went out of Egypt, the house of Jacob from a people of a foreign language;
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Judah was his sanctuary, [and] Israel his dominion.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The sea saw [it], and fled: Jordan was driven back.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 The mountains skipped like rams, [and] the little hills like lambs.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 What [ailed] thee, O thou sea, that thou fleddest? thou Jordan, [that] thou wast driven back?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ye mountains, [that] ye skipped like rams; [and] ye little hills, like lambs?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Tremble, thou earth, at the presence of the LORD, at the presence of the God of Jacob;
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Who turned the rock [into] a standing water, the flint into a fountain of waters.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalms 114 >