< Proverbs 26 >
1 As snow in summer, and as rain in harvest; so honor is not seemly for a fool.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 As the bird by wandering, as the swallow by flying, so the curse causeless shall not come.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 A whip for the horse, a bridle for the ass, and a rod for the fool's back.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Answer not a fool according to his folly, lest thou also be like him.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Answer a fool according to his folly, lest he be wise in his own conceit.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 He that sendeth a message by the hand of a fool cutteth off the feet, [and] drinketh damage.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 The legs of the lame are not equal: so [is] a parable in the mouth of fools.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 As he that bindeth a stone in a sling, so [is] he that giveth honor to a fool.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 [As] a thorn goeth up into the hand of a drunkard, so [is] a parable in the mouth of fools.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 The great [God] that formed all [things] both rewardeth the fool, and rewardeth transgressors.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 As a dog returneth to his vomit, [so] a fool returneth to his folly.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 Seest thou a man wise in his own conceit? [there is] more hope of a fool than of him.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 The slothful [man] saith, [There is] a lion in the way; a lion [is] in the streets.
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 [As] the door turneth upon its hinges, so [doth] the slothful upon his bed.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 The slothful hideth [his] hand in [his] bosom; it grieveth him to bring it again to his mouth.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 The sluggard [is] wiser in his own conceit than seven men that can render a reason.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 He that passeth by, [and] meddleth with strife [belonging] not to him, [is like] one that taketh a dog by the ears.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 As a mad [man] who casteth fire-brands, arrows, and death,
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 So [is] the man [that] deceiveth his neighbor, and saith, Am not I in sport?
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Where no wood is, [there] the fire goeth out: so where [there is] no tale-bearer, the strife ceaseth.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 [As] coals [are] to burning coals, and wood to fire; so [is] a contentious man to kindle strife.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 The words of a tale-bearer [are] as wounds, and they go down into the innermost parts of the belly.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 Burning lips and a wicked heart [are like] a potsherd covered with silver dross.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 He that hateth dissembleth with his lips, and layeth up deceit within him;
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 When he speaketh fair, believe him not: for [there are] seven abominations in his heart.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 [Whose] hatred is covered by deceit, his wickedness shall be shown before the [whole] congregation.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Whoever diggeth a pit shall fall into it: and he that rolleth a stone, it will return upon him.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 A lying tongue hateth [those that are] afflicted by it; and a flattering mouth worketh ruin.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.