< Proverbs 25 >

1 These [are] also proverbs of Solomon, which the men of Hezekiah king of Judah copied out.
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 [It is] the glory of God to conceal a thing: but the honor of kings [is] to search out a matter.
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 The heaven for hight, and the earth for depth, and the heart of kings [is] unsearchable.
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Take away the dross from the silver, and there shall come forth a vessel for the finer.
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Take away the wicked [from] before the king, and his throne shall be established in righteousness.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Put not forth thyself in the presence of the king, and stand not in the place of great [men]:
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 For better [it is] that it be said to thee, Come up hither; than that thou shouldst be put lower in the presence of the prince whom thy eyes have seen.
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 Go not forth hastily to strive, lest [thou know not] what to do in the end thereof, when thy neighbor hath put thee to shame.
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Debate thy cause with thy neighbor [himself]; and reveal not a secret to another:
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 Lest he that heareth [it] put thee to shame, and thy infamy turn not away.
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 A word fitly spoken [is like] apples of gold in pictures of silver.
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 [As] an ear-ring of gold, and an ornament of fine gold, [so is] a wise reprover upon an obedient ear.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 As the cold of snow in the time of harvest, [so is] a faithful messenger to them that send him: for he refresheth the soul of his masters.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Whoever boasteth himself of a false gift [is like] clouds and wind without rain.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 By long forbearing is a prince persuaded, and a soft tongue breaketh the bone.
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Hast thou found honey? eat so much as is sufficient for thee, lest thou be filled with it, and vomit it.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Withdraw thy foot from thy neighbor's house; lest he be weary of thee, and [so] hate thee.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 A man that beareth false witness against his neighbor [is] a maul, and a sword, and a sharp arrow.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Confidence in an unfaithful man in time of trouble [is like] a broken tooth, and a foot out of joint.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 [As] he that taketh away a garment in cold weather, [and as] vinegar upon nitre; so [is] he that singeth songs to a heavy heart.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 If thy enemy shall hunger, give him bread to eat; and if he shall thirst, give him water to drink:
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 For thou shalt heap coals of fire upon his head, and the LORD will reward thee.
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 The north wind driveth away rain: so [doth] an angry countenance a backbiting tongue.
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 [It is] better to dwell in a corner of the house-top, than with a brawling woman and in a wide house.
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 [As] cold waters to a thirsty soul, so [is] good news from a far country.
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 A righteous man falling down before the wicked [is as] a turbid fountain, and a corrupt spring.
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 [It is] not good to eat much honey: so [for men] to search their own glory [is not] glory.
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 He that [hath] no rule over his own spirit [is like] a city [that is] broken down, [and] without walls.
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< Proverbs 25 >