< Proverbs 24 >

1 Be not thou envious against evil men, neither desire to be with them.
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 For their heart studieth destruction, and their lips talk of mischief.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Through wisdom is a house built; and by understanding it is established:
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 And by knowledge shall the chambers be filled with all precious and pleasant riches.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 A wise man [is] strong; and a man of knowledge increaseth strength.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 For by wise counsel thou shalt make thy war: and in multitude of counselors [there is] safety.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Wisdom [is] too high for a fool: he openeth not his mouth in the gate.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 He that deviseth to do evil shall be called a mischievous person.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 The thought of foolishness [is] sin: and the scorner [is] an abomination to men.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 [If] thou faintest in the day of adversity, thy strength [is] small.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 If thou forbearest to deliver [them that are] drawn to death, and [those that are] ready to be slain;
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 If thou sayest, Behold, we knew it not; doth not he that pondereth the heart consider [it]? and he that keepeth thy soul, doth [not] he know [it]? and will [not] he render to [every] man according to his works?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 My son, eat thou honey, because [it is] good; and the honey-comb, [which is] sweet to thy taste:
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 So [shall] the knowledge of wisdom [be] to thy soul: when thou hast found [it], then there shall be a reward, and thy expectation shall not be cut off.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Lay not wait, O wicked [man], against the dwelling of the righteous; destroy not his resting-place:
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 For a just [man] falleth seven times, and riseth again: but the wicked shall fall into mischief.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Rejoice not when thy enemy falleth, and let not thy heart be glad when he stumbleth:
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Lest the LORD see [it], and it displease him, and he turn away his wrath from him.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Fret not thyself because of evil [men], neither be thou envious at the wicked;
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 For there shall be no reward to the evil [man]; the candle of the wicked shall be extinguished.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 My son, fear thou the LORD and the king: [and] meddle not with them that are given to change:
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 For their calamity shall rise suddenly; and who knoweth the ruin of them both?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 These [things] also [belong] to the wise. [It is] not good to have respect of persons in judgment.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 He that saith to the wicked, Thou [art] righteous; him shall the people curse, nations shall abhor him:
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 But to them that rebuke [him] shall be delight, and a good blessing shall come upon them.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 [Every man] shall kiss [his] lips that giveth a right answer.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Prepare thy work without, and make it fit for thyself in the field; and afterwards build thy house.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Be not a witness against thy neighbor without cause; and deceive [not] with thy lips.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Say not, I will do so to him as he hath done to me: I will render to the man according to his work.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 I went by the field of the slothful, and by the vineyard of the man void of understanding;
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 And lo, it was all grown over with thorns, [and] nettles had covered the face of it, and its stone wall was broken down.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Then I saw, [and] considered [it] well: I looked upon [it], [and] received instruction.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 [Yet] a little sleep, a little slumber, a little folding of the hands to sleep:
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 So shall thy poverty come [as] one that traveleth; and thy want as an armed man.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Proverbs 24 >