< Proverbs 16 >
1 The preparations of the heart in man, and the answer of the tongue, [are] from the LORD.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All the ways of a man [are] clean in his own eyes; but the LORD weigheth the spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Commit thy works to the LORD, and thy thoughts shall be established.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 The LORD hath made all [things] for himself: yes, even the wicked for the day of evil.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Every one [that is] proud in heart [is] an abomination to the LORD: [though] hand [join] in hand, he shall not be unpunished.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 By mercy and truth iniquity is purged: and by the fear of the LORD [men] depart from evil.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When a man's ways please the LORD, he maketh even his enemies to be at peace with him.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better [is] a little with righteousness, than great revenues without right.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 A man's heart deviseth his way: but the LORD directeth his steps.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 A divine sentence [is] in the lips of the king: his mouth transgresseth not in judgment.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 A just weight and balance [are] the LORD'S: all the weights of the bag [are] his work.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 [It is] an abomination to kings to commit wickedness: for the throne is established by righteousness.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Righteous lips [are] the delight of kings; and they love him that speaketh right.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 The wrath of a king [is as] messengers of death: but a wise man will pacify it.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the light of a king's countenance [is] life; and his favor [is] as a cloud of the latter rain.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 How much better [is it] to get wisdom than gold? and to get understanding rather to be chosen than silver?
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 The highway of the upright [is] to depart from evil: he that keepeth his way preserveth his soul.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Pride [goeth] before destruction, and a haughty spirit before a fall.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Better [it is to be] of a humble spirit with the lowly, than to divide the spoil with the proud.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 He that handleth a matter wisely shall find good: and whoever trusteth in the LORD, happy [is] he.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 The wise in heart shall be called prudent: and the sweetness of the lips increaseth learning.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Understanding [is] a well-spring of life to him that hath it: but the instruction of fools [is] folly.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of the wise teacheth his mouth, and addeth learning to his lips.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Pleasant words [are as] a honey-comb, sweet to the soul, and health to the bones.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way that seemeth right to a man, but the end of it [is] the ways of death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 He that laboreth laboreth for himself; for his mouth craveth it of him.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 An ungodly man diggeth up evil: and in his lips [there is] as a burning fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A froward man soweth strife: and a whisperer separateth chief friends.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 A violent man enticeth his neighbor, and leadeth him into the way [that is] not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 He shutteth his eyes to devise froward things: moving his lips he bringeth evil to pass.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 The hoary head [is] a crown of glory, [if] it is found in the way of righteousness.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 [He that is] slow to anger [is] better than the mighty; and he that ruleth his spirit, than he that taketh a city.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 The lot is cast into the lap: but the whole disposing of it [is] from the LORD.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.