< Numbers 4 >
1 And the LORD spoke to Moses and to Aaron, saying,
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Take the sum of the sons of Kohath from among the sons of Levi, after their families, by the house of their fathers;
“Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
3 From thirty years old and upward, even until fifty years old, all that enter into the host, to do the work in the tabernacle of the congregation.
Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
4 This [shall be] the service of the sons of Kohath in the tabernacle of the congregation, [about] the most holy things.
“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
5 And when the camp moveth forward, Aaron shall come, and his sons, and they shall take down the covering vail, and cover the ark of testimony with it:
Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
6 And shall put on it the covering of badgers' skins, and shall spread over [it] a cloth wholly of blue, and shall put in the staffs of it.
Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
7 And upon the table of show-bread they shall spread a cloth of blue, and put on it the dishes, and the spoons, and the bowls, and covers to cover with: and the continual bread shall be upon it.
“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
8 And they shall spread upon them a cloth of scarlet, and cover the same with a covering of badgers' skins, and shall put in the staffs of it.
Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
9 And they shall take a cloth of blue, and cover the candlestick of the light, and its lamps, and its tongs, and its snuff-dishes, and all its oil vessels, with which they minister to it:
“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
10 And they shall put it, and all its vessels, within a covering of badgers' skins, and shall put [it] upon a bar.
Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
11 And upon the golden altar they shall spread a cloth of blue, and cover it with a covering of badgers' skins, and shall put to it its staffs.
“Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
12 And they shall take all the instruments of ministry, with which they minister in the sanctuary, and put [them] in a cloth of blue, and cover them with a covering of badgers' skins, and shall put [them] on a bar.
“Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
13 And they shall take away the ashes from the altar, and spread a purple cloth upon it:
“Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
14 And they shall put upon it all its vessels, with which they minister about it, [even] the censers, the flesh-hooks, and the shovels, and the basins, all the vessels of the altar; and they shall spread upon it a covering of badgers' skins, and put to it its staffs.
Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
15 And when Aaron and his sons have made an end of covering the sanctuary, and all the vessels of the sanctuary, as the camp is to move forward; after that, the sons of Kohath shall come to bear [it]: but they shall not touch [any] holy thing, lest they die. These [things are] the burden of the sons of Kohath in the tabernacle of the congregation.
“Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
16 And to the office of Eleazar the son of Aaron the priest [pertain] the oil for the light, and the sweet incense, and the daily meat-offering, and the anointing oil, [and] the oversight of all the tabernacle, and of all that [is] in it, in the sanctuary, and in its vessels.
“Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
17 And the LORD spoke to Moses and to Aaron, saying,
Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
18 Cut ye not off the tribe of the families of the Kohathites from among the Levites:
“Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
19 But thus do to them, that they may live, and not die, when they approach to the most holy things: Aaron and his sons shall go in, and appoint them every one to his service and to his burden:
Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
20 But they shall not go in to see when the holy things are covered, lest they die.
Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
21 And the LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
22 Take also the sum of the sons of Gershon, throughout the house of their fathers, by their families;
“Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
23 From thirty years old and upward until fifty years old shalt thou number them; all that enter in to perform the service, to do the work in the tabernacle of the congregation.
Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
24 This [is] the service of the families of the Gershonites, to serve, and for burdens:
“Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
25 And they shall bear the curtains of the tabernacle, and the tabernacle of the congregation, its covering, and the covering of the badgers' skins that [is] above upon it, and the hanging for the door of the tabernacle of the congregation,
Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 And the hangings of the court, and the hanging for the door of the gate of the court, which [is] by the tabernacle and by the altar round about, and their cords, and all the instruments of their service, and all that is made for them: so shall they serve.
makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
27 At the appointment of Aaron and his sons shall be all the service of the sons of the Gershonites, in all their burdens, and in all their service: and ye shall appoint to them in charge all their burdens.
Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
28 This [is] the service of the families of the sons of Gershon in the tabernacle of the congregation: and their charge [shall be] under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.
Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
29 As for the sons of Merari, thou shalt number them after their families, by the house of their fathers;
“Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
30 From thirty years old and upward even to fifty years old shalt thou number them, every one that entereth into the service, to do the work of the tabernacle of the congregation.
Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
31 And this [is] the charge of their burden, according to all their service in the tabernacle of the congregation; the boards of the tabernacle, and its bars, and its pillars, and its sockets,
Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
32 And the pillars of the court round about, and their sockets, and their pins, and their cords, with all their instruments, and with all their service: and by name ye shall reckon the instruments of the charge of their burden.
ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
33 This [is] the service of the families of the sons of Merari, according to all their service, in the tabernacle of the congregation, under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.
Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
34 And Moses and Aaron and the chief of the congregation numbered the sons of the Kohathites after their families, and after the house of their fathers,
Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
35 From thirty years old and upward even to fifty years old, every one that entereth into the service, for the work in the tabernacle of the congregation:
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
36 And those that were numbered of them by their families were two thousand seven hundred and fifty.
atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
37 These [were] they that were numbered of the families of the Kohathites, all that might do service in the tabernacle of the congregation, whom Moses and Aaron numbered according to the commandment of the LORD by the hand of Moses.
Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
38 And those that were numbered of the sons of Gershon, throughout their families, and by the house of their fathers,
Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
39 From thirty years old and upward even to fifty years old, every one that entereth into the service, for the work in the tabernacle of the congregation,
Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
40 Even those that were numbered of them, throughout their families, by the house of their fathers, were two thousand and six hundred and thirty.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
41 These [are] they that were numbered of the families of the sons of Gershon, of all that might do service in the tabernacle of the congregation, whom Moses and Aaron numbered according to the commandment of the LORD.
Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
42 And those that were numbered of the families of the sons of Merari, throughout their families, by the house of their fathers,
Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
43 From thirty years old and upward even to fifty years old, every one that entereth into the service for the work in the tabernacle of the congregation,
Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
44 Even those that were numbered of them after their families, were three thousand and two hundred.
atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
45 These [are] those that were numbered of the families of the sons of Merari, whom Moses and Aaron numbered according to the word of the LORD by the hand of Moses.
Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
46 All those that were numbered of the Levites, whom Moses and Aaron and the chief of Israel numbered, after their families, and after the house of their fathers,
Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
47 From thirty years old and upward even to fifty years old, every one that came to do the service of the ministry, and the service of the burden in the tabernacle of the congregation,
Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
48 Even those that were numbered of them, were eight thousand and five hundred and eighty.
analipo 8,580.
49 According to the commandment of the LORD they were numbered by the hand of Moses, every one according to his service, and according to his burden: thus were they numbered by him, as the LORD commanded Moses.
Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.