< Nehemiah 10 >

1 Now those that sealed [were], Nehemiah, the Tirshatha, the son of Hachaliah, and Zidkijah,
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 Seraiah, Azariah, Jeremiah,
Seraya, Azariya, Yeremiya
3 Pashur, Amariah, Malchijah,
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Hattush, Shebaniah, Malluch,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harim, Meremoth, Obadiah,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniel, Ginnethon, Baruch,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Meshullam, Abijah, Mijamin,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Maaziah, Bilgai, Shemaiah: these [were] the priests.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 And the Levites: both Jeshua the son of Azaniah, Binnui of the sons of Henadad, Kadmiel;
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 And their brethren, Shebaniah, Hodijah, Kelita, Pelaiah, Hanan,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Micha, Rehob, Hashabiah,
Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zaccur, Sherebiah, Shebaniah,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Hodijah, Bani, Beninu,
Hodiya, Bani ndi Beninu.
14 The chief of the people; Parosh, Pahath-moab, Elam, Zatthu, Bani,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 Bunni, Azgad, Bebai,
Buni, Azigadi, Bebai,
16 Adonijah, Bigvai, Adin,
Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Ater, Hizkijah, Azzur,
Ateri, Hezekiya, Azuri,
18 Hodijah, Hashum, Bezai,
Hodiya, Hasumu, Bezayi
19 Hariph, Anathoth, Nebai,
Harifu, Anatoti, Nebayi,
20 Magpiash, Meshullam, Hezir,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Meshezabeel, Zadok, Jaddua,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
22 Pelatiah, Hanan, Anaiah,
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
23 Hoshea, Hananiah, Hashub,
Hoseya, Hananiya, Hasubu
24 Hallohesh, Pileha, Shobek,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehum, Hashabnah, Maaseiah,
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
26 And Ahijah, Hanan, Anan,
Ahiya, Hanani, Anani,
27 Malluch, Harim, Baanah.
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 And the rest of the people, the priests, the Levites, the porters, the singers, the Nethinims, and all they that had separated themselves from the people of the lands to the law of God, their wives, their sons, and their daughters, every one having knowledge, and having understanding;
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 They united with their brethren, their nobles, and entered into a curse, and into an oath, to walk in God's law, which was given by Moses the servant of God, and to observe and do all the commandments of the LORD our LORD, and his judgments and his statutes;
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 And that we would not give our daughters to the people of the land, nor take their daughters for our sons:
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 And [if] the people of the land should bring wares or any provisions on the sabbath day to sell, [that] we would not buy it of them on the sabbath, or on the holy day: and [that] we would leave the seventh year, and the exaction of every debt.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 Also we made ordinances for us, to charge ourselves yearly with the third part of a shekel for the service of the house of our God;
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 For the show-bread, and for the continual meat-offering, and for the continual burnt-offering, of the sabbaths, of the new moons, for the set feasts, and for the holy [things], and for the sin-offerings to make an atonement for Israel, and [for] all the work of the house of our God.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 And we cast the lots among the priests, the Levites, and the people, for the wood-offering, to bring [it] into the house of our God, after the houses of our fathers, at times appointed year by year, to burn upon the altar of the LORD our God, as [it is] written in the law:
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 And to bring the first-fruits of our ground, and the first-fruits of all fruit of all trees, year by year, to the house of the LORD:
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 Also the first-born of our sons, and of our cattle, as [it is] written in the law, and the firstlings of our herds and of our flocks, to bring to the house of our God, to the priests that minister in the house of our God:
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 And [that] we should bring the first-fruits of our dough, and our offerings, and the fruit of all manner of trees, of wine and of oil, to the priests, to the chambers of the house of our God; and the tithes of our ground to the Levites, that the same Levites might have the tithes in all the cities of our tillage.
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 And the priest the son of Aaron shall be with the Levites, when the Levites take tithes: and the Levites shall bring up the tenth of the tithes to the house of our God, to the chambers, into the treasure house.
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 For the children of Israel and the children of Levi shall bring the offering of the corn, of the new wine, and the oil, to the chambers, where [are] the vessels of the sanctuary, and the priests that minister, and the porters, and the singers: and we will not forsake the house of our God.
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”

< Nehemiah 10 >