< Leviticus 18 >

1 And the LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak to the children of Israel, and say to them, I [am] the LORD your God.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
3 After the doings of the land of Egypt in which ye dwelt, shall ye not do: and after the doings of the land of Canaan whither I bring you, shall ye not do: neither shall ye walk in their ordinances.
Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
4 Ye shall perform my judgments, and keep my ordinances, to walk in them; I [am] the LORD your God.
Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Ye shall therefore keep my statutes and my judgments: which if a man doeth, he shall live in them: I [am] the LORD.
Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
6 None of you shall approach to any that is near of kin to him, to uncover [their] nakedness: I am the LORD.
“‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
7 The nakedness of thy father, or the nakedness of thy mother, shalt thou not uncover: she [is] thy mother, thou shalt not uncover her nakedness.
“‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
8 The nakedness of thy father's wife shalt thou not uncover: it [is] thy father's nakedness.
“‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
9 The nakedness of thy sister, the daughter of thy father, or daughter of thy mother, [whether] born at home, or born abroad, [even] their nakedness thou shalt not uncover.
“‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
10 The nakedness of thy son's daughter, or of thy daughter's daughter, [even] their nakedness thou shalt not uncover: for theirs [is] thy own nakedness.
“‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
11 The nakedness of thy father's wife's daughter, begotten by thy father, (she [is] thy sister) thou shalt not uncover her nakedness.
“‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
12 Thou shalt not uncover the nakedness of thy father's sister: she [is] thy father's near kinswoman.
“‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
13 Thou shalt not uncover the nakedness of thy mother's sister: for she [is] thy mother's near kinswoman.
“‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
14 Thou shalt not uncover the nakedness of thy father's brother, thou shalt not approach to his wife: she [is] thy aunt.
“‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
15 Thou shalt not uncover the nakedness of thy daughter-in-law: she [is] thy son's wife, thou shalt not uncover her nakedness.
“‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
16 Thou shalt not uncover the nakedness of thy brother's wife: it [is] thy brother's nakedness.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
17 Thou shalt not uncover the nakedness of a woman and her daughter, neither shalt thou take her son's daughter, or her daughter's daughter, to uncover her nakedness; [for] they [are] her near kinswomen: it [is] wickedness.
“‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
18 Neither shalt thou take a wife to her sister, to vex [her], to uncover her nakedness besides the other in her life -[time].
“‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
19 Also thou shalt not approach to a woman to uncover her nakedness, as long as she is put apart for her uncleanness.
“‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
20 Moreover, thou shalt not lie carnally with thy neighbor's wife, to defile thyself with her.
“‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
21 And thou shalt not let any of thy seed pass through [the fire] to Molech, neither shalt thou profane the name of thy God: I [am] the LORD.
“‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
22 Thou shalt not lie with mankind, as with womankind: it [is] abomination.
“‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
23 Neither shalt thou lie with any beast to defile thyself therewith: neither shall any woman stand before a beast to lie down thereto: it [is] confusion.
“‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
24 Defile not ye yourselves in any of these things; for in all these the nations are defiled which I cast out before you:
“‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
25 And the land is defiled: therefore I do visit its iniquity upon it, and the land itself vomiteth out her inhabitants.
Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
26 Ye shall therefore keep my statutes and my judgments, and shall not commit [any] of these abominations; [neither] any of your own nation, nor any stranger that sojourneth among you.
Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
27 (For all these abominations have the men of the land done, who [were] before you, and the land is defiled; )
pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
28 That the land may not vomit you out also, when ye defile it, as it vomited out the nations that [were] before you.
Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
29 For whoever shall commit any of these abominations, even the souls that commit [them] shall be cut off from among their people.
“‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
30 Therefore shall ye keep my ordinance, that [ye] commit not [any one] of these abominable customs, which were committed before you, and that ye defile not yourselves in them; I [am] the LORD your God.
Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< Leviticus 18 >