< Lamentations 5 >
1 Remember, O LORD, what is come upon us: consider, and behold our reproach.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Our inheritance is turned to strangers, our houses to aliens.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 We are orphans and fatherless, our mothers [are] as widows.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 We have drank our water for money; our wood is sold to us.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Our necks [are] under persecution: we labor, [and] have no rest.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 We have given the hand [to] the Egyptians, [and to] the Assyrians, to be satisfied with bread.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Our fathers have sinned, [and are] not; and we have borne their iniquities.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Servants have ruled over us: [there is] none that doth deliver [us] out of their hand.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 We procured our bread with [the peril of] our lives, because of the sword of the wilderness.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Our skin was black like an oven because of the terrible famine.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 They ravished the women in Zion, [and] the maids in the cities of Judah.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Princes were hanged by their hand: the faces of elders were not honored.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 They took the young men to grind, and the children fell under the wood.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 The elders have ceased from the gate, the young men from their music.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 The joy of our heart hath ceased; our dance is turned into mourning.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 The crown is fallen [from] our head: woe to us, that we have sinned!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 For this our heart is faint; for these [things] our eyes are dim.
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 Because of the mountain of Zion, which is desolate, the foxes walk upon it.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Thou, O LORD, remainest for ever; thy throne from generation to generation.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Why dost thou forget us for ever, [and] forsake us so long time?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Turn thou us to thee, O LORD, and we shall be turned; renew our days as of old.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 But thou hast utterly rejected us; thou art very wroth against us.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.