< Job 32 >
1 So these three men ceased to answer Job, because he [was] righteous in his own eyes.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Then was kindled the wrath of Elihu the son of Barachel the Buzite, of the kindred of Ram: against Job was his wrath kindled, because he justified himself rather than God.
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 Also against his three friends was his wrath kindled, because they had found no answer, and [yet] had condemned Job.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Now Elihu had waited till Job had spoken because they [were] older than he.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 When Elihu saw that [there was] no answer in the mouth of [these] three men, then his wrath was kindled.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 And Elihu the son of Barachel the Buzite answered and said, I [am] young, and ye [are] very old; wherefore I was afraid, and durst not show you my opinion.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 I said, Days should speak, and multitude of years should teach wisdom.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 But [there is] a spirit in man: and the inspiration of the Almighty giveth them understanding.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 Great men are not [always] wise: neither do the aged understand judgment.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Therefore I said, Hearken to me; I also will show my opinion.
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Behold, I waited for your words; I gave ear to your reasons, whilst ye searched out what to say.
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Yes, I attended to you, and behold, [there was] none of you that convinced Job, [or] that answered his words:
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Lest ye should say, We have found out wisdom: God thrusteth him down, not man.
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Now he hath not directed [his] words against me: neither will I answer him with your speeches.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 They were amazed, they answered no more: they left off speaking.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 When I had waited, (for they spoke not, but stood still, [and] answered no more; )
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 [I said], I will answer also my part, I also will show my opinion.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 For I am full of matter, the spirit within me constraineth me.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Behold, my belly [is] as wine [which] hath no vent; it is ready to burst like new bottles.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 I will speak, that I may be refreshed: I will open my lips and answer.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Let me not, I pray you, accept any man's person, neither let me give flattering titles to man.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 For I know not to give flattering titles; [in so doing], my Maker would soon take me away.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”