< Job 31 >

1 I Made a covenant with my eyes; why then should I think upon a maid?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 For what portion of God [is there] from above? and [what] inheritance of the Almighty from on high?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 [Is] not destruction to the wicked? and a strange [punishment] to the workers of iniquity?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Doth not he see my ways, and count all my steps?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 If I have walked with vanity, or if my foot hath hasted to deceit;
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Let me be weighed in an even balance, that God may know my integrity.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 If my step hath turned out of the way, and my heart walked after my eyes, and if any blot hath cleaved to my hands;
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 [Then] let me sow, and let another eat; yes, let my offspring be rooted out.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 If my heart hath been deceived by a woman, or [if] I have laid wait at my neighbor's door;
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 [Then] let my wife grind to another, and let others bow down upon her.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 For this [is] a hainous crime; yea, it [is] an iniquity [to be punished by] the judges.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 For it [is] a fire [that] consumeth to destruction, and would root out all my increase.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 If I despised the cause of my man-servant or of my maid-servant, when they contended with me;
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 What then shall I do when God riseth up? and when he visiteth, what shall I answer him?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Did not he that made me in the womb make him? and did not one fashion us in the womb?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 If I have withheld the poor from [their] desire, or have caused the eyes of the widow to fail;
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Or have eaten my morsel myself alone, and the fatherless hath not eaten of it;
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 (For from my youth he was brought up with me, as [with] a father, and I have guided her from my mother's womb; )
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 If I have seen any perish for want of clothing, or any poor without covering;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 If his loins have not blessed me, and [if] he hath not been warmed with the fleece of my sheep;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 If I have lifted up my hand against the fatherless, when I saw my help in the gate:
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 [Then] let my arm fall from my shoulder-blade, and my arm be broken from the bone.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 For destruction [from] God [was] a terror to me, and by reason of his highness I could not endure.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 If I have made gold my hope, or have said to the fine gold, [Thou art] my confidence;
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 If I have rejoiced because my wealth [was] great, and because my hand had gained much;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 If I have beheld the sun when it shined, or the moon walking [in] brightness;
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 And my heart hath been secretly enticed, or my mouth hath kissed my hand:
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 This also [were] an iniquity [to be punished by] the judge: for I should have denied the God [that is] above.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 If I have rejoiced at the destruction of him that hated me, or have lifted up myself when evil found him:
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Neither have I suffered my mouth to sin by wishing a curse to his soul.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 If the men of my tabernacle have not said, Oh that we had of his flesh! we cannot be satisfied.
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 The stranger did not lodge in the street: [but] I opened my doors to the traveler.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 If I have covered my transgressions as Adam, by hiding my iniquity in my bosom:
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Did I fear a great multitude, or did the contempt of families terrify me, that I kept silence, [and] went not out of the door?
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Oh that one would hear me! behold, my desire [is], [that] the Almighty would answer me, and [that] my adversary had written a book.
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Surely I would take it upon my shoulder, [and] bind it [as] a crown to me.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 I would declare to him the number of my steps; as a prince would I go near to him.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 If my land crieth against me, or its furrows likewise complain;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 If I have eaten the fruits of it without money, or have caused its owners to lose their life:
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Let thistles grow instead of wheat, and cockle instead of barley. The words of Job are ended.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >