< Job 20 >

1 Then answered Zophar the Naamathite, and said,
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Therefore do my thoughts cause me to answer, and for [this] I make haste.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 I have heard the check of my reproach, and the spirit of my understanding causeth me to answer.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Knowest thou [not] this of old, since man was placed upon earth,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 That the triumphing of the wicked [is] short, and the joy of the hypocrite [but] for a moment?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Though his excellence shall mount up to the heavens, and his head reach to the clouds;
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 [Yet] he shall perish for ever like his own dung: they who have seen him shall say, Where [is] he?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 He shall fly away as a dream, and will not be found: yea, he shall be chased away as a vision of the night.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 The eye also [which] saw him shall [see him] no more; neither shall his place any more behold him.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 His children shall seek to please the poor, and his hands shall restore their goods.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 His bones are full [of the sin] of his youth, which shall lie down with him in the dust.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Though wickedness may be sweet in his mouth, [though] he may hide it under his tongue;
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 [Though] he may spare it, and forsake it not; but keep it still within his mouth:
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 [Yet] his food in his bowels is turned, [it is] the gall of asps within him.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 He hath swallowed down riches, and he shall vomit them up again: God shall cast them out of his belly.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 He shall suck the poison of asps: the viper's tongue shall slay him.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 He shall not see the river, the floods, the brooks of honey and buttermilk.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 That which he labored for shall he restore, and shall not swallow [it]: according to [his] substance [shall] the restitution [be], and he shall not rejoice [in it].
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Because he hath oppressed [and] hath forsaken the poor; [because] he hath violently taken away a house which he did not build.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Surely he shall not feel quietness in his belly, he shall not save of that which he desired.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 There shall none of his food be left; therefore shall no man look for his goods.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 In the fullness of his sufficiency he shall be in straits: every hand of the wicked shall come upon him.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 [When] he is about to fill his belly, [God] shall cast the fury of his wrath upon him, and shall rain [it] upon him while he is eating.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 He shall flee from the iron weapon, [and] the bow of steel shall strike him through.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 It is drawn, and cometh out of the body; yes, the glittering sword cometh out of his gall: terrors [are] upon him.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 All darkness [shall be] hid in his secret places: a fire not blown shall consume him; it shall go ill with him that is left in his tabernacle.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 The heaven shall reveal his iniquity; and the earth shall rise up against him.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 The increase of his house shall depart, [and his goods] shall flow away in the day of his wrath.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 This [is] the portion of a wicked man from God, and the heritage appointed to him by God.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >