< Isaiah 45 >

1 Thus saith the LORD to his anointed, to Cyrus, whose right hand I have held to subdue nations before him; and I will loose the loins of kings, to open before him the two-leaved gates, and the gates shall not be shut;
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 I will go before thee, and make the crooked places straight: I will break in pieces the gates of brass, and cut asunder the bars of iron:
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 And I will give thee the treasures of darkness, and hidden riches of secret places, that thou mayest know that I, the LORD, who call [thee] by thy name, [am] the God of Israel.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 For Jacob my servant's sake, and Israel my elect, I have even called thee by thy name: I have surnamed thee, though thou hast not known me:
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 I [am] the LORD, and [there is] none else, [there is] no God besides me: I girded thee, though thou hast not known me:
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 That they may know from the rising of the sun, and from the west, that [there is] none besides me. I [am] the LORD, and [there is] none else.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 I form the light, and create darkness: I make peace, and create evil: I the LORD do all these [things].
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Drop down, ye heavens, from above, and let the skies pour down righteousness: let the earth open, and let them bring forth salvation, and let righteousness spring up together; I the LORD have created it.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Woe to him that contendeth with his Maker! [Let] the potsherd [contend] with the potsherds of the earth. Shall the clay say to him that fashioneth it, What makest thou? or thy work, He hath no hands?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Woe to him that saith to [his] father, What begettest thou? or to the woman, What hast thou brought forth?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Thus saith the LORD, the Holy One of Israel, and his Maker, Ask me of things to come concerning my sons, and concerning the work of my hands command ye me.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 I have made the earth, and created man upon it: I, [even] my hands, have stretched out the heavens, and all their host have I commanded.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 I have raised him up in righteousness, and I will direct all his ways: he shall build my city, and he shall let go my captives, not for price nor reward, saith the LORD of hosts.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Thus saith the LORD, The labor of Egypt, and merchandise of Cush and of the Sabeans, men of stature, shall come over to thee, and they shall be thine: they shall come after thee; in chains they shall come over, and they shall fall down to thee, they shall make supplication to thee, [saying], Surely God [is] in thee; and [there is] none else, [there is] no God.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Verily thou [art] a God that hidest thyself, O God of Israel, the Savior.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 They shall be ashamed, and also confounded, all of them: they shall go to confusion together [that are] makers of idols.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 [But] Israel shall be saved in the LORD with an everlasting salvation: ye shall not be ashamed nor confounded world without end.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 For thus saith the LORD that created the heavens; God himself that formed the earth and made it; he hath established it, he created it not in vain, he formed it to be inhabited: I [am] the LORD; and [there is] none else.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 I have not spoken in secret, in a dark place of the earth: I have not said to the seed of Jacob, Seek ye me in vain: I the LORD speak righteousness, I declare things that are right.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Assemble yourselves and come; draw near together, ye [that have] escaped of the nations: they have no knowledge that set up the wood of their graven image, and pray to a god [that] cannot save.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Tell ye, and bring [them] near; yes, let them take counsel together: who hath declared this from ancient time? [who] hath told it from that time? [have] not I the LORD? and [there is] no God else besides me; a just God and a Savior; [there is] none besides me.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Look to me, and be ye saved, all the ends of the earth: for I [am] God, and [there is] none else.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 I have sworn by myself, the word is gone out of my mouth [in] righteousness, and shall not return, That to me every knee shall bow, every tongue shall swear.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Surely, shall [one] say, in the LORD have I righteousness and strength: [even] to him shall [men] come; and all that are incensed against him shall be ashamed.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 In the LORD shall all the seed of Israel be justified, and shall glory.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Isaiah 45 >