< Habakkuk 1 >

1 The burden which Habakkuk the prophet saw.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 O LORD, how long shall I cry, and thou wilt not hear! [even] cry out to thee [of] violence, and thou wilt not save!
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Why dost thou show me iniquity, and cause [me] to behold grievance? for devastation and violence [are] before me: and there are [that] raise strife and contention.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Therefore the law is slackened, and judgment doth never go forth: for the wicked doth encompass the righteous; therefore wrong judgment proceedeth.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Behold ye among the heathen, and regard, and wonder marvelously: for [I] will work a work in your days, [which] ye will not believe though it be told [you].
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 For lo, I raise up the Chaldeans, [that] bitter and hasty nation, which shall march through the breadth of the land, to possess the dwelling-places [that are] not theirs.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 They [are] terrible and dreadful: their judgment and their dignity shall proceed from themselves.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Their horses also are swifter than the leopards, and are more fierce than the evening wolves: and their horsemen shall spread themselves, and their horsemen shall come from far; they shall fly as the eagle [that] hasteth to eat.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 They shall come all for violence: their faces shall sup up [as] the east wind, and they shall gather the captivity as the sand.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 And they shall scoff at the kings, and the princes shall be a scorn to them: they shall deride every strong hold; for they shall heap dust, and take it.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Then shall [his] mind change, and he shall pass over, and offend, [imputing] this his power to his god.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 [Art] thou not from everlasting, O LORD my God, my Holy One? We shall not die. O LORD, thou hast ordained them for judgment; and O mighty God, thou hast established them for correction.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 [Thou art] of purer eyes than to behold evil, and canst not look on iniquity: why lookest thou on them that deal treacherously, [and] keepest silence when the wicked devoureth [the man that is] more righteous than he?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 And makest men as the fishes of the sea, as the creeping animals [that have] no ruler over them?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 They take up all of them with the angle, they catch them in their net, and gather them in their drag: therefore they rejoice and are glad.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Therefore they sacrifice to their net, and burn incense to their drag; because by them their portion [is] fat, and their food plenteous.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Shall they therefore empty their net, and not spare continually to slay the nations?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Habakkuk 1 >