< Exodus 9 >

1 Then the LORD said to Moses, Go in to Pharaoh, and tell him, Thus saith the LORD God of the Hebrews, Let my people go, that they may serve me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 For if thou shalt refuse to let [them] go, and wilt hold them still,
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 Behold, the hand of the LORD is upon thy cattle which are in the field, upon the horses, upon the asses, upon the camels, upon the oxen, and upon the sheep: [there shall be] a very grievous murrain.
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 And the LORD shall sever between the cattle of Israel, and the cattle of Egypt: and there shall nothing die of all [that] belongs to the children of Israel.
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 And the LORD appointed a set time, saying, To-morrow the LORD will do this thing in the land.
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 And the LORD did that thing on the morrow, and all the cattle of Egypt died: but of the cattle of the children of Israel died not one.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 And Pharaoh sent, and behold, there was not one of the cattle of the Israelites dead. And the heart of Pharaoh was hardened, and he did not let the people go.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 And the LORD said to Moses and to Aaron, Take to you handfuls of ashes of the furnace, and let Moses sprinkle it towards heaven in the sight of Pharaoh.
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 And it shall become small dust in all the land of Egypt, and shall be a boil breaking forth [with] blains upon man, and upon beast, throughout all the land of Egypt.
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 And they took ashes of the furnace, and stood before Pharaoh; and Moses sprinkled it towards heaven; and it became a boil breaking forth [with] blains upon man, and upon beast.
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 And the magicians could not stand before Moses, because of the boil: for the boil was upon the magicians, and upon all the Egyptians.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 And the LORD hardened the heart of Pharaoh, and he hearkened not to them; as the LORD had spoke to Moses.
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 And the LORD said to Moses, Rise early in the morning, and stand before Pharaoh, and say to him, Thus saith the LORD God of the Hebrews, Let my people go, that they may serve me.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 For I will at this time send all my plagues upon thy heart, and upon thy servants, and upon thy people: that thou mayest know that [there is] none like me in all the earth.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 For now I will stretch out my hand, that I may smite thee and thy people with pestilence; and thou shalt be cut off from the earth.
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 And in very deed for this [cause] have I raised thee up, to show [in] thee my power; and that my name may be declared throughout all the earth.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 As yet dost thou exalt thyself against my people, that thou wilt not let them go?
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 Behold, to-morrow about this time I will cause it to rain a very grievous hail, such as hath not been in Egypt since its foundation even until now.
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 Send therefore now, [and] gather thy cattle, and all that thou hast in the field: [for upon] every man and beast which shall be found in the field, and shall not be brought home, the hail shall come down upon them, and they shall die.
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 He that feared the word of the LORD, among the servants of Pharaoh, made his servants and his cattle flee into the houses:
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 And he that regarded not the word of the LORD, left his servants and his cattle in the field.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 And the LORD said to Moses, Stretch forth thy hand towards heaven, that there may be hail in all the land of Egypt, upon man, and upon beast, and upon every herb of the field, throughout the land of Egypt.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 And Moses stretched forth his rod towards heaven, and the LORD sent thunder and hail, and the fire ran along upon the ground: and the LORD rained hail upon the land of Egypt.
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 So there was hail, and fire mingled with the hail, very grievous, such as there had been none like it in all the land of Egypt, since it became a nation.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 And the hail smote, throughout all the land of Egypt, all that [was] in the field, both man and beast, and the hail smote every herb of the field and broke every tree of the field.
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 Only in the land of Goshen, where the children of Israel [were], there was no hail.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 And Pharaoh sent, and called for Moses and Aaron, and said to them, I have sinned this time: the LORD [is] righteous, and I and my people [are] wicked.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 Entreat the LORD (for [it is] enough) that there be no [more] mighty thunderings and hail; and I will let you go, and ye shall stay no longer.
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 And Moses said to him, As soon as I am gone out of the city, I will spread abroad my hands to the LORD; [and] the thunder shall cease, neither shall there be any more hail; that thou mayest know how that the earth [is] the LORD'S.
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 But as for thee and thy servants, I know that ye will not yet fear the LORD God.
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 And the flax and the barley were smitten: for the barley [was] in the ear, and the flax [was] bolled.
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 But the wheat and the rye were not smitten; for they [were] not grown up.
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 And Moses went out of the city from Pharaoh, and spread abroad his hands to the LORD: and the thunders and hail ceased, and the rain was not poured upon the earth.
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 And when Pharaoh saw that the rain and the hail and the thunders had ceased, he sinned yet more, and hardened his heart, he and his servants.
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 And the heart of Pharaoh was hardened, neither would he let the children of Israel go; as the LORD had spoken by Moses.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.

< Exodus 9 >