< 1 Samuel 6 >

1 And the ark of the LORD was in the country of the Philistines seven months.
Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
2 And the Philistines called for the priests and the diviners, saying, What shall we do to the ark of the LORD? tell us with what we shall send it to its place.
Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
3 And they said, If ye send away the ark of the God of Israel, send it not empty; but in any wise return him a trespass-offering: then ye will be healed, and it will be known to you why his hand is not removed from you.
Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
4 Then said they, What [shall be] the trespass-offering which we shall return to him? They answered, Five golden emerods, and five golden mice, [according to] the number of the lords of the Philistines: for one plague [was] on you all, and on your lords.
Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
5 Wherefore ye shall make images of your emerods, and images of your mice that mar the land; and ye shall give glory to the God of Israel: it may be he will lighten his hand from off you, and from off your gods, and from off your land.
Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
6 Why then do ye harden your hearts, as the Egyptians and Pharaoh hardened their hearts? when he had wrought wonderfully among them, did they not let the people go, and they departed?
Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
7 Now therefore make a new cart, and take two milch-cows on which there hath come no yoke, and tie the cows to the cart, and bring their calves home from them:
“Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
8 And take the ark of the LORD, and lay it upon the cart; and put the jewels of gold which ye return to him [for] a trespass-offering, in a coffer by its side; and send it away, that it may go.
Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
9 And see, if it goeth up by the way of his own coast to Beth-shemesh, [then] he hath done us this great evil: but if not, then we shall know, that [it is] not his hand [that] smote us; it [was] a chance [that] happened to us.
Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
10 And the men did so; and took two milch cows, and tied them to the cart, and shut up their calves at home:
Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
11 And they laid the ark of the LORD upon the cart, and the coffer with the mice of gold and the images of their emerods.
Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
12 And the cows took the straight way to the way of Beth-shemesh, [and] went along the highway, lowing as they went, and turned not aside [to] the right hand or [to] the left; and the lords of the Philistines went after them to the border of Beth-shemesh.
Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
13 And [they of] Beth-shemesh [were] reaping their wheat harvest in the valley: and they lifted up their eyes, and saw the ark, and rejoiced to see [it].
Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
14 And the cart came into the field of Joshua, a Beth-shemite, and stood there, where [there was] a great stone: and they cleaved the wood of the cart, and offered the cows a burnt-offering to the LORD.
Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
15 And the Levites took down the ark of the LORD, and the coffer that [was] with it, in which [were] the jewels of gold, and put [them] on the great stone: and the men of Beth-shemesh offered burnt-offerings and sacrificed sacrifices the same day to the LORD.
Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
16 And when the five lords of the Philistines had seen [it], they returned to Ekron the same day.
Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
17 And these [are] the golden emerods which the Philistines returned [for] a trespass-offering to the LORD; for Ashdod one, for Gaza one, for Askelon one, for Gath one, for Ekron one;
Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
18 And the golden mice, [according to] the number of all the cities of the Philistines [belonging] to the five lords, [both] of fortified cities, and of country villages, even to the great [stone of] Abel, on which they set down the ark of the LORD: [which stone remaineth] to this day in the field of Joshua the Beth-shemite.
Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
19 And he smote the men of Beth-shemesh, because they had looked into the ark of the LORD, even he smote of the people fifty thousand and seventy men: and the people lamented, because the LORD had smitten [many] of the people with a great slaughter.
Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
20 And the men of Beth-shemesh said, Who is able to stand before this holy LORD God? and to whom shall he go up from us?
Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
21 And they sent messengers to the inhabitants of Kirjath-jearim, saying, The Philistines have brought again the ark of the LORD; come ye down, [and] bring it up to you.
Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”

< 1 Samuel 6 >