< Psalms 118 >
1 O give thanks to the LORD; for he is good: because his mercy endureth for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Let Israel now say, that his mercy endureth for ever.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Let the house of Aaron now say, that his mercy endureth for ever.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Let them now that fear the LORD say, that his mercy endureth for ever.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 I called upon the LORD in distress: the LORD answered me, and set me in a large place.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 The LORD is on my side; I will not fear: what can man do to me?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 The LORD taketh my part with them that help me: therefore shall I see my desire upon them that hate me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 It is better to trust in the LORD than to put confidence in man.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 It is better to trust in the LORD than to put confidence in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations surrounded me: but in the name of the LORD will I destroy them.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They surrounded me; yea, they surrounded me: but in the name of the LORD I will destroy them.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They surrounded me like bees; they are quenched as the fire of thorns: for in the name of the LORD I will destroy them.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Thou hast violently thrust at me that I might fall: but the LORD helped me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 The LORD is my strength and song, and is become my salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 The voice of rejoicing and salvation is in the tabernacles of the righteous: the right hand of the LORD doeth valiantly.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of the LORD is exalted: the right hand of the LORD doeth valiantly.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I shall not die, but live, and declare the works of the LORD.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 The LORD hath chastened me greatly: but he hath not given me over to death.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open to me the gates of righteousness: I will enter them, and I will praise the LORD:
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This gate of the LORD, into which the righteous shall enter.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I will praise thee: for thou hast heard me, and art become my salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 The stone which the builders refused is become the head stone of the corner.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 This is the LORD’S doing; it is marvellous in our eyes.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This is the day which the LORD hath made; we will rejoice and be glad in it.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Save now, I beseech thee, O LORD: O LORD, I beseech thee, send now prosperity.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed be he that cometh in the name of the LORD: we have blessed you out of the house of the LORD.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 God is the LORD, who hath shown us light: bind the sacrifice with cords, even to the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Thou art my God, and I will praise thee: thou art my God, I will exalt thee.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 O give thanks to the LORD; for he is good: for his mercy endureth for ever.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.