< Job 19 >
1 Then Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 How long will ye vex my soul, and break me in pieces with words?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 These ten times have ye reproached me: ye are not ashamed that ye make yourselves strange to me.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And be it indeed that I have erred, my error remaineth with myself.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 If indeed ye will magnify yourselves against me, and plead against me my reproach:
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Know now that God hath overthrown me, and hath surrounded me with his net.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Behold, I cry out of wrong, but I am not heard: I cry aloud, but there is no judgment.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 He hath fenced up my way that I cannot pass, and he hath set darkness in my paths.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 He hath stripped me of my glory, and taken the crown from my head.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He hath destroyed me on every side, and I am gone: and my hope hath he removed like a tree.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 He hath also kindled his wrath against me, and he counteth me to him as one of his enemies.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 His troops come together, and raise up their way against me, and encamp around my tent.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 He hath put my brethren far from me, and my acquaintance are verily estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 My kinsmen have failed, and my familiar friends have forgotten me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 They that dwell in my house, and my maids, count me for a stranger: I am an alien in their sight.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 I called my servant, and he gave me no answer; I entreated him with my mouth.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 My breath is strange to my wife, though I make supplication to the children of my own body.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Yea, young children despised me; I arose, and they spoke against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 All my close friends abhorred me: and they whom I loved are turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 My bone cleaveth to my skin and to my flesh, and I have escaped with the skin of my teeth.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Have pity upon me, have pity upon me, O ye my friends; for the hand of God hath touched me.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why do ye persecute me as God, and are not satisfied with my flesh?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 O that my words were now written! O that they were printed in a book!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 That they were engraved with an iron pen in lead in the rock for ever!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 For I know that my redeemer liveth, and that he shall stand at the latter day upon the earth:
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And though after my skin worms destroy this body, yet in my flesh shall I see God:
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Whom I shall see for myself, and my eyes shall behold, and not another; though my reins be consumed within me.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 But ye should say, Why persecute we him, seeing the root of the matter is found in me?
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Be ye afraid of the sword: for wrath bringeth the punishments of the sword, that ye may know there is a judgment.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”