< Job 18 >
1 Then answered Bildad the Shuhite, and said,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 How long will it be ere ye make an end of words? mark, and afterwards we will speak.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Why are we counted as beasts, and reputed vile in your sight?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 He teareth himself in his anger: shall the earth be forsaken for thee? and shall the rock be removed out of its place?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Yea, the light of the wicked shall be put out, and the spark of his fire shall not shine.
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 The light shall be dark in his tent, and his lamp shall be put out with him.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 The steps of his strength shall be shortened, and his own counsel shall cast him down.
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 For he is cast into a net by his own feet, and he walketh upon a snare.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 The trap shall take him by the heel, and the robber shall prevail against him.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 The snare is laid for him in the ground, and a trap for him in the way.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Terrors shall make him afraid on every side, and shall drive him to his feet.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 His strength shall be hungerbitten, and destruction shall be ready at his side.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 It shall devour the strength of his skin: even the firstborn of death shall devour his strength.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 His confidence shall be rooted out of his tent, and it shall bring him to the king of terrors.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 It shall dwell in his tent, because it is none of his: brimstone shall be scattered upon his habitation.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 His roots shall be dried up beneath, and above shall his branch be cut off.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 The remembrance of him shall perish from the earth, and he shall have no name in the street.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 He shall be driven from light into darkness, and chased out of the world.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 He shall neither have son nor nephew among his people, nor any remaining in his dwellings.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 They that come after him shall be appalled at his day, as they that went before were seized with horror.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Surely such are the dwellings of the wicked, and this is the place of him that knoweth not God.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”