< Deuteronomy 14 >

1 Ye are the children of the LORD your God: ye shall not cut yourselves, nor make any baldness between your eyes for the dead.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 For thou art an holy people to the LORD thy God, and the LORD hath chosen thee to be a special people to himself, above all the nations that are upon the earth.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 Thou shalt not eat any abominable thing.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 These are the beasts which ye shall eat: the ox, the sheep, and the goat,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 The hart, and the roebuck, and the fallow deer, and the wild goat, and the pygarg, and the wild ox, and the chamois.
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 And every beast that parteth the hoof, and cleaveth the cleft into two claws, and cheweth the cud among the beasts, that ye shall eat.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Nevertheless these ye shall not eat of them that chew the cud, or of them that divide the cloven hoof; the camel, and the hare, and the coney: for they chew the cud, but divide not the hoof; therefore they are unclean to you.
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 And the swine, because it divideth the hoof, yet cheweth not the cud, is unclean to you: ye shall not eat of their flesh, nor touch their dead carcase.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 These ye shall eat of all that are in the waters: all that have fins and scales shall ye eat:
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 And whatever hath not fins and scales ye may not eat; it is unclean to you.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Of all clean birds ye shall eat.
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 But these are they of which ye shall not eat: the eagle, and the ossifrage, and the ospray,
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 And the glede, and the kite, and the vulture after his kind,
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 And every raven after his kind,
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 And the owl, and the night hawk, and the cuckow, and the hawk after his kind,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 The little owl, and the great owl, and the swan,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 And the pelican, and the gier eagle, and the cormorant,
tsekwe, vuwo, dembo,
18 And the stork, and the heron after her kind, and the lapwing, and the bat.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 And every creeping thing that flieth is unclean to you: they shall not be eaten.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 But of all clean fowls ye may eat.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 Ye shall not eat of any thing that dieth of itself: thou shalt give it to the stranger that is in thy gates, that he may eat it; or thou mayest sell it to an alien: for thou art an holy people to the LORD thy God. Thou shalt not boil a kid in his mother’s milk.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 Thou shalt truly tithe all the increase of thy seed, that the field bringeth forth year by year.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 And thou shalt eat before the LORD thy God, in the place which he shall choose to place his name there, the tithe of thy grain, of thy wine, and of thy oil, and the firstlings of thy herds and of thy flocks; that thou mayest learn to fear the LORD thy God always.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 And if the way is too long for thee, so that thou art not able to carry it; or if the place is too far from thee, which the LORD thy God shall choose to set his name there, when the LORD thy God hath blessed thee:
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 Then shalt thou turn it into money, and bind up the money in thy hand, and shalt go to the place which the LORD thy God shall choose:
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 And thou shalt bestow that money for whatever thy soul desireth, for oxen, or for sheep, or for wine, or for strong drink, or for whatever thy soul desireth: and thou shalt eat there before the LORD thy God, and thou shalt rejoice, thou, and thy household,
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 And the Levite that is within thy gates; thou shalt not forsake him; for he hath no part nor inheritance with thee.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 At the end of three years thou shalt bring forth all the tithe of thy increase the same year, and shalt lay it up within thy gates:
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 And the Levite, (because he hath no part nor inheritance with thee, ) and the stranger, and the fatherless, and the widow, who are within thy gates, shall come, and shall eat and be satisfied; that the LORD thy God may bless thee in all the work of thy hand which thou doest.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

< Deuteronomy 14 >